LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb21 March tsa. 7
  • Funsani Mafunso

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Funsani Mafunso
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Nkhani Zofanana
  • Afikeni Pamtima Anthu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Seŵenzetsani Mawu a Mulungu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Landilani Thandizo la Yehova Kupitila M’pemphelo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Thandizani Maphunzilo a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
mwb21 March tsa. 7
M’bale na mkazi wake akugaŵila kathirakiti pa ulaliki wa kasitandi mu sitesheni yapansi ya sitima.

CITANI KHAMA PA ULALIKI | WONJEZELANI CIMWEMWE CANU MU ULALIKI

Funsani Mafunso

Yehova, “Mulungu wacimwemwe,” amafuna kuti tizipeza cimwemwe mu ulaliki. (1 Tim. 1:11) Cimwemwe cathu cimawonjezeka ngati tikulitsa maluso athu mu ulaliki. Kufunsa mafunso kumautsa cidwi ca munthu. Komanso ni njila yabwino yoyambitsila makambilano. Mafunso amalimbikitsa anthu kuganiza. (Mat. 22:41-45) Ngati tifunsa munthu mafunso na kumumvetsela, timakhala ngati tikumuuza kuti, ‘Ndiwe wofunika kwa ine.’ (Yak. 1:19) Mayankho amene munthu angapeleke angatithandize kudziŵa mmene tingakambile naye kuti timufike pa mtima.

ONELELANI VIDIYO YAKUTI PEZANI CIMWEMWE PA NCHITO YOPANGA OPHUNZILA—NOLANI MALUSO ANU—KUFUNSA MAFUNSO, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • Mbali ya vidiyo yakuti, ‘Pezani Cimwemwe pa Nchito Yopanga Ophunzila—Nolani Maluso Anu—Kufunsa Mafunso.’ Rose akupatsa mayi wacikulile mpando wake mu sitima.

    Ni makhalidwe abwino ati amene Rose anaonetsa?

  • Mbali ya vidiyo yakuti, ‘Pezani Cimwemwe pa Nchito Yopanga Ophunzila—Nolani Maluso Anu—Kufunsa Mafunso.’ Neeta akupeleka moni kwa Rose na kudzidziwikitsa.

    Kodi mlongo Neeta anaseŵenzetsa bwanji mafunso poonetsa cidwi kwa womvetsela wake?

  • Mbali ya vidiyo yakuti, ‘Pezani Cimwemwe pa Nchito Yopanga Ophunzila—Nolani Maluso Anu—Kufunsa Mafunso.’ Rose akuyankha funso limene Neeta wamufunsa.

    Kodi Neeta anaseŵenzetsa bwanji mafunso pothandiza Rose kukulitsa cidwi comvetsela uthenga wabwino?

  • Mbali ya vidiyo yakuti, ‘Pezani Cimwemwe pa Nchito Yopanga Ophunzila—Nolani Maluso Anu—Kufunsa Mafunso.’ Neeta akufunsa funso Rose pambuyo poŵelenga lemba.

    Kodi Neeta anagwilitsila nchito bwanji mafunso pothandiza Rose kuganizilapo pa zimene anali kukambilana naye?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani