LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp24 na. 1 masa. 6-9
  • Baibo Ni Gwelo la Malangizo Odalilika

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Baibo Ni Gwelo la Malangizo Odalilika
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila) —2024
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • TIMAFUNIKILA MALANGIZO OCOKELA KWA MULUNGU
  • BAIBO IMATIUZA ZIMENE MULUNGU AMAFUNA KUTI TIZICITA
  • 12 Zolinga
    Galamuka!—2018
  • N’ciani Cingatithandize Kukhala na Tsogolo Labwino?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
  • Kodi Inu Mudzatsatila Malangizo a Ndani?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila) —2024
  • Thandizo Ilipo
    Galamuka!—2020
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila) —2024
wp24 na. 1 masa. 6-9

Baibo Ni Gwelo la Malangizo Odalilika

Ngati timangoyendela maganizo athu kapena a anthu ena posankha zocita, sitingakhale otsimikiza kuti zimene tikucitazo zidzakhala na zotulukapo zabwino. Baibo imafotokoza cifukwa cake zili conco. Koma ilinso na malangizo odalilika amene angatithandize kukhala na umoyo wabwino.

TIMAFUNIKILA MALANGIZO OCOKELA KWA MULUNGU

M’Baibo, Yehovaa Mulungu amatiuza kuti sanalenge anthu kuti azidzitsogolela okha, koma kuti azidalila iye kuti aŵatsogolele. (Yeremiya 10:23) Ndiye cifukwa cake anapeleka malangizo abwino opezeka m’Baibo. Iye amatikonda ife anthu, ndipo safuna kuti tipange zisankho zolakwika zimene zingatibweletsele mavuto aakulu pa umoyo wathu. (Deuteronomo 5:29; 1 Yohane 4:8) Komanso iye angatipatse malangizo abwino kwambili cifukwa ni Mlengi wathu, ndipo ali na nzelu kwambili komanso amadziŵa zambili. (Salimo 100:3; 104:24) Komabe, Mulungu sakakamiza anthu kuti azitsatila mfundo zake za makhalidwe abwino.

Yehova anapatsa mwamuna na mkazi woyamba, Adamu na Hava, zonse zimene anali kufunikila kuti akhale na cimwemwe ceniceni. (Genesis 1:​28, 29; 2:​8, 15) Anaŵapatsanso malangizo osavuta, ndipo anali kufuna kuti iwo aziwatsatila. Komabe, anaŵalola kudzisankhila okha kaya kutsatila malangizowo kapena ayi. (Genesis 2:​9, 16, 17) N’zacisoni kuti Adamu na Hava anasankha kutsatila zofuna zawo m’malo motsatila miyezo ya Mulungu. (Genesis 3:6) Kodi pakhala zotulukapo zotani? Kodi anthu lomba ali na umoyo wacimwemwe cifukwa cokhala na ufulu wocita ciliconse cimene aona kuti n’cabwino? Kutalitali! M’kupita kwa zaka, zadziŵika kuti kunyalanyaza miyezo ya Mulungu sikubweletsa mtendele weniweni kapena cimwemwe.—Mlaliki 8:9.

Baibo ili na malangizo amene angatithandize kupanga zisankho mwanzelu, mosasamala kanthu za kumene tikhala. (2 Timoteyo 3:​16, 17; onani bokosi lakuti “Buku la Anthu Onse.”) Onani mmene imatithandizila.

Onani cifukwa cake m’poyenela kunena kuti Baibo ni “Mawu a Mulungu.”—1 Atesalonika 2:13. Tambani vidiyo yakuti Ndani Analemba Baibulo? pa jw.org.

BUKU LA ANTHU ONSE

Mulungu ni Mlengi wathu wanzelu komanso wacikondi. N’cifukwa cake wapatsa aliyense mwayi wolandila malangizo ake amene ali m’Baibo. Onani mfundo zotsatilazi ponena za Baibo:

Anthu a mitundu yosiyana-siyana akuŵelenga Baibo. Cithunzi cionetsanso Mabaibo opulitiwa komanso a zipangizo.
  • 3,500+ Ici ni ciŵelengelo ca zinenelo zimene Baibo yathunthu kapena mbali yake imapezeka. Palibe buku lina limene lamasulilidwa m’zinenelo zambili kuposa Baibo.

  • 5,000,000,000+ Ici ni ciŵelengelo ca Mabaibo onse amene afalitsidwa. Palibe buku lina limene linafalitsidwa kwambili kuposa Baibo m’mbili yonse ya anthu.

Baibo sikweza mtundu, dziko, fuko, kapena cikhalidwe cina ciliconse kuposa cinzake. Ndithudi ni buku la anthu onse!

Ŵelengani Baibo ya pa intaneti (yopezeka m’zinenelo zoposa 250) pa jw.org.

Mwamuna akuseŵenzetsa cala poŵelenga Baibo.

CIFUKWA CAKE ANTHU ENA SAIKHULUPILILA BAIBO

Anthu ena amakamba kuti malangizo a m’Baibo si odalilika. Iwo amakamba zinthu ngati izi:

Ena Amati: “Baibo imadzitsutsa.”

Zoona Zake: Poyamba, nkhani zina za m’Baibo zingaoneke monga n’zosagwilizana. Koma mukamvetsa nkhani yonse, kumene inalembedwela, nthawi pamene inalembedwa, maganizo a wolemba nkhaniyo, komanso mfundo zina, mudzatha kuona kuti n’zogwilizana.

Kuti muoneko zitsanzo, ŵelengani nkhani yakuti, “Kodi Nkhani za m’Baibulo Zimatsutsana?” pa jw.org.

Ena Amati: “Anthu amene amati amakhulupilila Baibo amacita zoipa. Conco malangizo a m’Baibo si abwino.”

Zoona Zake: Anthu ena amene amati amakhulupilila Baibo amacita zoipa cifukwa cosatsatila ziphunzitso zake. Koma sikuti Baibo ndiyo ili na vuto. Inakambilatu kuti anthu ambili, kuphatikizapo atsogoleli acipembedzo, amene amati amatsatila Baibo adzayamba kucita zosiyana na zimene imaphunzitsa. Inakambanso kuti pa cifukwa ici, anthu azidzalankhula “monyoza ziphunzitso za m’Baibo.”—2 Petulo 2:​1, 2.

Kuti muone citsanzo cimodzi ca mmene atsogoleli ambili a cipembedzo apatukila pa zimene Baibo imaphunzitsa, ŵelengani nkhani yakuti “Kodi Cipembedzo Casanduka Bizinesi Yotentha?” pa jw.org ku Chichewa.

Ena Amati: “Anthu amene amakhulupilila Baibo sakhala ololela.”

Zoona Zake: Baibo imatilimbikitsa kulemekeza anthu ena. Imaletsa makhalidwe otsatilawa:

  • kudziona wofunika kwambili kuposa anthu ena.—Afilipi 2:3.

  • kusalemekeza anthu cifukwa ca makhalidwe awo kapena zimene amakhulupilila.—1 Petulo 2:17.

  • kukakamiza ena kuyendela maganizo athu.—Mateyu 10:14.

Baibo imaonetsa kuti nthawi zonse, Mulungu amacita zinthu mokoma mtima komanso mwacilungamo na anthu. Ndipo amafuna kuti nafenso tizicita cimodzimodzi.—Aroma 9:14.

Kuti mudziŵe zambili, ŵelengani nkhani yakuti “Kodi Baibo Imathandiza Bwanji Anthu Kukhala Ololela?” pa jw.org.

BAIBO IMATIUZA ZIMENE MULUNGU AMAFUNA KUTI TIZICITA

Baibo imatiuza mmene Yehova wakhala akucitila zinthu na anthu kucokela pa ciyambi. Zomwe zili m’Baibo zimatithandiza kudziŵa zimene Mulungu amaona kuti n’zoyenela kapena zosayenela, zothandiza kapena zovulaza. (Salimo 19:​7, 11) Mfundo zake sizikutha mphamvu, ndipo zingatithandize kusankha zinthu mwanzelu pa nkhani ya coyenela na cosayenela.

Mwacitsanzo, onani ulangizi wa pa Miyambo 13:20 umene umati: “Munthu woyenda ndi anthu anzelu adzakhala wanzelu, koma amene amacita zinthu ndi anthu opusa adzapeza mavuto.” Mfundo imeneyi inali yothandiza m’nthawi yakale. Ndipo masiku anonso ni yothandiza. Baibo ni yodzala na malangizo ofunika komanso othandiza ngati amenewa.—Onani bokosi lakuti “Malangizo a m’Baibo Sakutha Mphamvu.”

Mungafunse kuti, ‘Kodi ningatsimikize bwanji kuti malangizo a m’Baibo ni othandiza masiku ano?’ Nkhani yotsatila ifotokoza mmene Baibo yathandizila anthu ena.

a Yehova ndilo dzina la Mulungu.—Salimo 83:18.

MALANGIZO A M’BAIBO SAKUTHA MPHAMVU

Ngakhale kuti papita zaka pafupifupi 2,000 kucokela pamene Baibo inatha kulembedwa, mfundo zake n’zothandizabe masiku ano. Cibadwa cathu sicinasinthe. Timafunabe kukhala na umoyo wabwino komanso wacimwemwe. (Mlaliki 1:9) Mfundo za m’Baibo zingatithandize kukhala na umoyo wotelo.

Kuona Mtima

  • “Tikufuna kucita zinthu zonse moona mtima.”—Aheberi 13:18.

  • “Munthu wakuba asiye kubako, koma azigwila nchito molimbikila.”—Aefeso 4:28.

Mocitila Zinthu na Anthu

  • “Aliyense asamangofuna zopindulitsa iyeyo basi, koma zopindulitsanso ena.”—1 Akorinto 10:24.

  • “Pitilizani kulolelana ndi kukhululukilana ndi mtima wonse.”—Akolose 3:13.

Kupanga Zisankho

  • “Munthu amene sadziŵa zambili amakhulupilila mawu alionse, koma wocenjela amaganizila zotsatila za zimene akufuna kucita.”—Miyambo 14:15.

  • “Munthu wocenjela akaona tsoka amabisala, koma wosadziŵa zinthu amangopitabe ndipo amakumana ndi mavuto.”—Miyambo 22:3.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani