Mande, August 25
Ngakhale kuti Khristuyo simunamuonepo, mumamukonda.—1 Pet. 1:8.
Yesu analimbana na mayeselo osiyanasiyana ocokela kwa Satana, kuphatikizapo ciyeso comuuza mwacindunji kuti aleke kukhala wokhulupilika kwa Mulungu. (Mat. 4:1-11) Satana anali wotsimikiza mtima kucimwitsa Yesu kuti asathe kupeleka dipo. Yesu anakumananso na mayeso ena pocita utumiki wake pa dziko lapansi. Anazunzidwa, ndipo moyo wake unali paciopsezo. (Luka 4:28, 29; 13:31) Anali kupililanso zophophonya za otsatila ake. (Maliko 9:33, 34) Pozengedwa mlandu kuti aphedwe, anazunzidwa na kunyozedwa. Ndipo anaphedwa m’njila yoŵaŵa komanso yonyazitsa kwambili. (Aheb. 12:1-3) Anapilila yekha mavuto othela popanda Yehova kum’teteza. (Mat. 27:46) Kunena zoona, Yesu anavutika zedi kuti apeleke dipo. Ndipo tikaganizila zinthu zimene Yesu anapitamo modzipeleka kaamba ka ife, cikondi cathu pa iye cimakula. w24.01 10-11 ¶7-9
Ciŵili, August 26
Onse amene amacita zinthu mopupuluma amasauka.—Miy. 21:5.
Kuleza mtima kumatithandiza pocita zinthu na anthu ena. Kumatithandiza kumvetsela modekha ena akamalankhula. (Yak. 1:19) Kuleza mtima kumalimbikitsanso mtendele. Kumatiteteza kuti tisacite zinthu mopupuluma, na kukamba zinthu zosayenela tikapanikizika maganizo. Ndipo tikakhala oleza mtima, sitidzakwiya msanga wina akatikhumudwitsa. M’malo mobwezela, ‘tidzapitiliza kulolelana na kukhululukilana ndi mtima wonse.’ (Akol. 3:12, 13) Kuleza mtima kungatithandizenso kupanga zisankho zabwino. M’malo modya mfulumila, tidzapatula nthawi yofufuza na kusanthula zisankhozo kuti tione zimene zili zabwino koposa. Mwacitsanzo, tikamafuna-funa nchito, tingafulumile kuvomela nchito iliyonse imene yapezeka. Komabe, tikakhala oleza mtima, tidzakhala pansi na kuganizila mmene idzakhudzila banja lathu na umoyo wathu wauzimu. Tikakhala oleza mtima, tidzapewa kupanga zisankho zoipa. w23.08 22 ¶8-9
Citatu, August 27
Ndimaona lamulo lina mʼthupi langa likumenyana ndi malamulo amʼmaganizo mwanga nʼkundicititsa kukhala kapolo wa lamulo la ucimo limene lili mʼthupi langa.—Aroma 7:23.
Ngati mungalefuke poona kuti mumakhala na zilakolako zoipa, kuganizila lonjezo limene munapeleka kwa Yehova podzipatulila kudzakuthandizani kutsimikiza mtima kugonjetsa mayeselo. Ndipo zoona zake n’zakuti lumbilo lanu la kudzipatulila lidzakuthandizani kugonjetsa mayeselo. Motani? Mukadzipatulila kwa Yehova mumadzikana nokha. Izi zikutanthauza kunena kuti toto ku zikhumbo zanu, na zolinga zanu zimene sizingakondweletse Yehova. (Mat. 16:24) Conco, mukakumana na mayeso simudzacedwa na kuganizilapo zimene muyenela kucita. Mudzakhala mutadziwilatu zocita, zomwe ni kukhalabe wokhulupilika kwa Yehova. Mudzakhalabe wosasunthika pa kukondweletsa Yehova. Mudzakhala ngati Yobu amene ngakhale pambuyo pokumana na mavuto aakulu ananena motsimikiza kuti: “Sindidzasiya kukhala wokhulupilika.”—Yobu 27:5. w24.03 9 ¶6-7