LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Sondo, September 14

Muthe kumvetsa bwino m’lifupi ndi m’litali, kukwela ndi kuzama kwa coonadi.​—Aef. 3:18.

Mukafuna kugula nyumba mungafune kudzionela nokha nyumbayo, kuizungulila na kuona milingo yake yonse. Tiyenela kucita cimodzi-modzi poŵelenga na kuphunzila Baibo. Mukamaŵelenga mothamanga, mungadziŵe mfundo zocepa cabe​—“mfundo zoyambilila za m’mawu opatulika a Mulungu.” (Aheb. 5:12) M’malo mwake, monga mmene mungacitile na nyumba, “fufuzani” kuti mumvetse mfundo zamtengo wapatali. Njila yabwino koposa yoŵelengela mawu a Mulungu ni kuyesa kuona mmene mfundo zosiyana-siyana zikugwilizanila. Muziyesetsa kumvetsa zimene mumakhulupilila komanso cifukwa cake mumazikhulupilila. Kuti timvetse Mawu a Mulungu, tiyenela kuŵelenga mfundo zozama za coonadi. Mtumwi Paulo analimbikitsa Akhristu anzake kuti ayenela kuŵelenga Mawu a Mulungu mwakhama ‘kuti athe kudziŵa bwino m’lifupi ndi m’litali ndi kukwela ndi kuzama’ kwa coonadi. Kucita zimenezi kunawathandiza ‘kuti azike mizu mokhazikika’ pa cikhulupililo. (Aef. 3:14-19) Ifenso tiyenela kucita cimodzi-modzi. w23.10 18 ¶1-3

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Mande, September 15

Abale, pa nkhani ya kumva zowawa ndi kuleza mtima, tengelani citsanzo ca aneneli amene analankhula mʼdzina la Yehova.​—Yak. 5:10.

M’Baibo, muli zitsanzo zambili za anthu amene anali oleza mtima. Conco, mungadziikile colinga coŵelenga zitsanzo zimenezo pa phunzilo la inu mwini. Mwacitsanzo, ngakhale kuti Davide anadzozedwa akali wacicepele kukhala mfumu yam’tsogolo ya Isiraeli, anayembekezela kwa zaka zambili kuti ayambe kulamulila. Nayenso Simiyoni komanso Anna anatumikila Yehova mokhulupilika poyembekezela Mesiya wolonjezedwayo. (Luka 2:25, 36-38) Mukamaŵelenga nkhani ngati zimenezi, muziyesa kupeza mayankho pa mafunso awa: N’ciyani cinathandiza munthu ameneyu kukhala woleza mtima? Kodi kuleza mtima kunam’pindulila motani? Nanga ningatengele bwanji citsanzo cake? Tingatengenso cenjezo pa zitsanzo za anthu amene sanali oleza mtima. (1 Sam. 13:8-14) Mungadzifunse kuti: ‘N’ciyani cinapangitsa kuti asakhale oleza mtima? Nanga anakumana na mavuto otani?’ w23.08 25 ¶15

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Ciŵili, September 16

Ife takhulupilila ndipo tadziŵa kuti inu ndinu Woyela amene Mulungu anamutumiza.​—Yoh. 6:69.

Mtumwi Petulo anali wokhulupilika, ndipo sanalole ciliconse kumulepheletsa kutsatila Yesu. Pa nthawi ina, anaonetsa kukhulupilika kwake pamene Yesu anakamba zinthu zimene ophunzila ake sanadzimvetse. (Yoh. 6:68) M’malo mopempha Yesu kuti awafotokozele tanthauzo lake, anthu ambili analeka kum’tsatila. Koma Petulo sanatelo. Iye anazindikila kuti Yesu yekhayo ndiye ali na “mawu amoyo wosatha.” Yesu anadziŵa kuti Petulo na atumwi ena adzam’thaŵa. Ngakhale n’telo, anali na cidalilo mwa Petulo cakuti iye adzabwelela na kukhalabe wokhulupilika. (Luka 22:31, 32) Yesu anamvetsa kuti “mzimu ndi wofunitsitsa, koma thupi ndi lofooka.” (Maliko 14:38) Ngakhale kuti Petulo anam’kana, Yesu sanam’taye mtumwi wake ameneyu. Ndipo iye ataukitsidwa, anaonekela kwa Petulo, amene mwacionekele anali yekha. (Maliko 16:7; Luka 24:34; 1 Akor. 15:5) Tangoganizilani mmene zinam’limbikitsila mtumwi wacisoniyo! w23.09 22 ¶9-10

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani