Cinayi, September 18
Nthawi zonse tizitamanda Mulungu kudzela mwa Yesu. Kucita zimenezi kuli ngati nsembe imene tikupeleka kwa Mulungu ndipo timagwilitsa nchito milomo yathu polengeza dzina lake.—Aheb. 13:15.
Masiku ano Akhristu onse ali na mwayi wopeleka nsembe kwa Yehova mwa kuseŵenzetsa nthawi yawo, mphamvu zawo, komanso cuma cawo, popititsa patsogolo ucifumu wa Mulungu. Tingaonetse kuti timayamikila mwayi wathu wolambila Yehova mwa kum’patsa nsembe zabwino koposa. Mtumwi Paulo, anachula zinthu zina zimene sitifunika kunyalanyaza pa kulambila kwathu. (Aheb. 10:22-25) Zimenezi ziphatikizapo kumufikila Yehova m’pemphelo, kulengeza poyela ciyembekezo cathu, kusonkhana pamodzi monga mpingo, komanso kulimbikitsana ‘makamaka pamene tikuona kuti tsiku la [Yehova] likuyandikila.’ Cakumapeto kwa buku la Chivumbulutso, mngelo wa Yehova anachula mawu akuti: “Lambilani Mulungu” kaŵili konse pofuna kuwagogomezela! (Chiv. 19:10; 22:9) Tiyeni ticite zonse zotheka kuti tisaiŵale mfundo yozama ya coonadi yonena za kacisi wauzimu wa Yehova, komanso mwayi wamtengo wapatali umene tili nawo wolambila Mulungu wathu wamkulu! w23.10 29 ¶17-18
Cisanu, September 19
[Pitilizani] kukondana.—1 Yoh. 4:7.
Tonse timafuna kuti “tipitilize kukondana.” Komabe, m’pofunika kwambili kukumbukila cenjezo la Yesu lakuti “cikondi ca anthu ambili cidzazilala.” (Mat. 24:12) Yesu sanatanthauze kuti izi zidzacitika pa mlingo waukulu pakati pa ophunzila ake. Ngakhale n’telo, tiyenela kukhala osamala kuti tisasoceletsedwe na kupanda cikondi kwa m’dzikoli. Tili na mfundo imeneyi m’maganizo, tiyeni tione funso lofunika kwambili ili: Kodi pali njila imene tingadziŵile ngati cikondi cathu pa abale cikali colimba? Njila imodzi imene tingadziŵile ngati cikondi cathu cikali colimba, ni kuona mmene timasamalila zocitika zina mu umoyo wathu. (2 Akor. 8:8) Cocitika cimodzi cinachulidwa na mtumwi Petulo. Iye anati: “Koposa zonse, khalani okondana kwambili, pakuti cikondi cimakwilila macimo oculuka.” (1 Pet. 4:8) Conco, zifooko komanso kupanda ungwilo kwa ena zingatithandize kudziŵa ngati cikondi cathu pa iwo cikali colimba. w23.11 10-11 ¶12-13
Ciŵelu, September 20
Muzikondana.—Yoh. 13:34.
Sitingamvele lamulo la Yesu lakuti tizikondana ngati timakonda ena mu mpingo na kupewa kukonda ena. Monga mmene zinalili kwa Yesu, nafenso sitingakhale omasuka kwa onse. (Yoh. 13:23; 20:2) Koma mtumwi Petulo akutikumbutsa kuti tiyenela kuyesetsa ‘kukonda gulu lonse la abale,’ cifukwa ni mbali ya banja lathu. (1 Pet. 2:17) Petulo anatilimbikitsa kuti tiyenela ‘kukondana kwambili kucokela mu mtima.’ (1 Pet. 1:22) Palembali, mawu akuti kukonda “kwambili” aphatikizapo kuonetsa cikondi kwa munthu wina ngakhale kuti zingakhale zovuta kucita zimenezo. Mwacitsanzo, ngati m’bale watikhumudwitsa m’njila ina yake, mwacibadwa tingafune kubwezela m’malo moonetsa cikondi. Komabe, Petulo anaphunzila kuti kubwezela sikukondweletsa Mulungu. (Yoh. 18:10, 11) Petulo analemba kuti: “Osabwezela coipa pa coipa kapena cipongwe pa cipongwe, koma m’malomwake muzidalitsa.” (1 Pet. 3:9) Lolani cikondi kukusonkhezelani kukhala okoma mtima komanso oganizila ena. w23.09 28-29 ¶9-11