Mande, September 8
Muzilemekeza anthu amene akugwila nchito mwakhama pakati panu, amenenso amakutsogolelani mwa Ambuye.—1 Ates. 5:12.
Pamene mtumwi Paulo analemba kalatayi, mpingo wa Atesalonika unali usanakwanitse caka. N’kutheka kuti amuna apaudindo mumpingowo anali acatsopano, ndipo anali kulakwitsa zina. Ngakhale n’telo, anayenela kulemekezedwa. Pamene cisautso cacikulu cikuyandikila, tidzafunika kudalila kwambili citsogozo ca akulu kuposa kale lonse. Nthawi zina sizingatheke kulandila malangizo ocokela ku likulu lathu kapena ku ofesi ya nthambi. Conco, m’pofunika kwambili palipano kuphunzila kuwakonda akulu na kuwalemekeza. Kaya pacitike zotani, tiyeni tikhalebe oganiza bwino, na kupewa kuyang’ana zophophonya zawo. M’malo mwake, tiziika maganizo athu pa mfundo yakuti Yehova kudzela mwa Khristu, akutsogolela amuna okhulupilika amenewa. Monga mmene cisoti cimatetezela mutu wa msilikali, naconso ciyembekezo cathu cacipulumutso cimateteza maganizo athu. Timaona kuti zimene dzikoli limapeleka n’zopanda phindu. (Afil. 3:8) Cimatithandizanso kukhala odekha komanso osasunthika. w23.06 11-12 ¶11-12
Ciŵili, September 9
Mkazi wopusa amakhala wolongolola. Iye ndi wopelewela nzelu.—Miy. 9:13.
Amene amamva ciitano ca “mkazi wopusa,” amafunika kusankha kaya kulabadila ciitanoco kapena ayi. Tili na zifukwa zomveka zopewela khalidwe laciwelewele. “Mkazi wopusa” akunena kuti: “Madzi akuba amatsekemela.”(Miy. 9:17) Kodi “madzi akuba” n’ciyani? Baibo imayelekezela kugonana pakati pa mwamuna na mkazi wake na madzi otsitsimula. (Miy. 5:15-18) Kugonana kumasangalatsa ngati kucitika pakati pa mwamuna na mkazi okwatilana mwalamulo. Komabe, izi n’zosiyana kutalitali na “madzi akuba,” omwe angatanthauze ciwelewele. Nthawi zambili, ciwelewele cimacitika usiku, monga mbala imene kambili imaba usiku. “Madzi akuba” angaoneke otsekemela maka-maka ngati ocita ciwelewele cimeneco amaona kuti palibe adzadziŵa. Ati kudzinamiza kwake ŵati! Yehova amaona zonse. Ndipo palibe coŵaŵa kwambili kuposa kutaya ciyanjo cake. Conco, palibenso ‘cotsekemela’ ngakhale pang’ono.—1 Akor. 6:9, 10. w23.06 22 ¶7-9
Citatu, September 10
Ngakhale nditacita mokakamizika, ndinebe woyangʼanila mogwilizana ndi udindo umene ndinapatsidwa.—1 Akor. 9:17.
Nanga bwanji ngati mwaona kuti mapemphelo anu komanso utumiki wanu zikungocitika mwa mwambo cabe? Ngati zaconco zakucitikilani pambuyo pa ubatizo, musaganize kuti basi mzimu wa Yehova wakucokelani. Ndinu wopanda ungwilo, ndipo nthawi zina mungamamve conco. Ngati cangu canu cayamba kucepa, muzisinkhasinkha citsanzo ca mtumwi Paulo. Ngakhale kuti anali kuyesetsa kutengela citsanzo ca Yesu, iye anadziŵa kuti nthawi zina sangakhale na cikhumbo cofuna kucita zimenezo. Paulo anali wotsimikiza mtima kukwanilitsa utumiki wake mosasamala kanthu za mmene anali kumvela pa nthawiyo. Mofananamo, musadalile maganizo anu opanda ungwilo popanga zisankho. Khalani otsimikiza kucita zoyenela mosasamala kanthu za mmene mukumvela.—1 Akor. 9:16. w24.03 11-12 ¶12-13