Ciŵili, September 9
Mkazi wopusa amakhala wolongolola. Iye ndi wopelewela nzelu.—Miy. 9:13.
Amene amamva ciitano ca “mkazi wopusa,” amafunika kusankha kaya kulabadila ciitanoco kapena ayi. Tili na zifukwa zomveka zopewela khalidwe laciwelewele. “Mkazi wopusa” akunena kuti: “Madzi akuba amatsekemela.”(Miy. 9:17) Kodi “madzi akuba” n’ciyani? Baibo imayelekezela kugonana pakati pa mwamuna na mkazi wake na madzi otsitsimula. (Miy. 5:15-18) Kugonana kumasangalatsa ngati kucitika pakati pa mwamuna na mkazi okwatilana mwalamulo. Komabe, izi n’zosiyana kutalitali na “madzi akuba,” omwe angatanthauze ciwelewele. Nthawi zambili, ciwelewele cimacitika usiku, monga mbala imene kambili imaba usiku. “Madzi akuba” angaoneke otsekemela maka-maka ngati ocita ciwelewele cimeneco amaona kuti palibe adzadziŵa. Ati kudzinamiza kwake ŵati! Yehova amaona zonse. Ndipo palibe coŵaŵa kwambili kuposa kutaya ciyanjo cake. Conco, palibenso ‘cotsekemela’ ngakhale pang’ono.—1 Akor. 6:9, 10. w23.06 22 ¶7-9
Citatu, September 10
Ngakhale nditacita mokakamizika, ndinebe woyangʼanila mogwilizana ndi udindo umene ndinapatsidwa.—1 Akor. 9:17.
Nanga bwanji ngati mwaona kuti mapemphelo anu komanso utumiki wanu zikungocitika mwa mwambo cabe? Ngati zaconco zakucitikilani pambuyo pa ubatizo, musaganize kuti basi mzimu wa Yehova wakucokelani. Ndinu wopanda ungwilo, ndipo nthawi zina mungamamve conco. Ngati cangu canu cayamba kucepa, muzisinkhasinkha citsanzo ca mtumwi Paulo. Ngakhale kuti anali kuyesetsa kutengela citsanzo ca Yesu, iye anadziŵa kuti nthawi zina sangakhale na cikhumbo cofuna kucita zimenezo. Paulo anali wotsimikiza mtima kukwanilitsa utumiki wake mosasamala kanthu za mmene anali kumvela pa nthawiyo. Mofananamo, musadalile maganizo anu opanda ungwilo popanga zisankho. Khalani otsimikiza kucita zoyenela mosasamala kanthu za mmene mukumvela.—1 Akor. 9:16. w24.03 11-12 ¶12-13
Cinayi, September 11
Asonyezeni kuti mumawakonda.—2 Akor. 8:24.
Tingawaonetse cikondi abale na alongo athu pokhala nawo pa ubwenzi. (2 Akor. 6:11-13) Ambili tili m’mipingo muli abale na alongo a zikhalidwe zosiyana-siyana, komanso zibadwa zosiyana-siyana. Tingakulitse cikondi cathu kwa onsewo mwa kuyang’ana kwambili pa makhalidwe awo abwino. Tikamaona ena mmene Yehova amawaonela, timaonetsa kuti timawakonda. Pa cisautso cacikulu, cikondi cidzakhala cofunika kwambili. Kodi n’kuti kumene tidzapeza citetezo cisautsoco cikadzayamba? Onani malangizo amene Yehova anauza atumiki ake Babulo wakale ataukilidwa. Iye anawauza kuti: “Inu anthu anga, pitani mukaloŵe m’zipinda zanu zamkati ndipo mukatseke zitseko. Mukabisale kwa kanthawi mpaka mkwiyo utadutsa.” (Yes. 26:20) Zioneka kuti malangizo amenewa adzagwilanso nchito kwa ife pa cisautso cacikulu. w23.07 6-7 ¶14-16