LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lff phunzilo 28
  • Muziyamikila pa Zimene Yehova na Yesu Anakucitilani

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Muziyamikila pa Zimene Yehova na Yesu Anakucitilani
  • Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • KUMBANI MOZAMILAPO
  • CIDULE CAKE
  • FUFUZANI
  • Cifukwa Cake Timacita Mgonelo wa Ambuye
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Zimene Mwambo Wosalila Zambili Umatiphunzitsa Ponena za Mfumu Yathu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
  • Cifukwa Cake Timapezeka pa Cikumbutso
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Yehova Amadalitsa Kuyesetsa Kwathu Kuti Ticite Cikumbutso
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
Onaninso Zina
Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
lff phunzilo 28
Phunzilo 28. Anthu akupatsilana mbale ya mkate wopanda cofufumitsa pa Mgonelo wa Ambuye.

PHUNZILO 28

Muziyamikila pa Zimene Yehova na Yesu Anakucitilani

Yopulinta
Yopulinta
Yopulinta

Kodi mungamve bwanji ngati mnzanu wakupatsani mphatso yabwino kwambili? Mwacidziŵikile mungakondwele ngako, ndipo mungamuyamikile cifukwa ca mphatso imeneyo. Yehova na Yesu anatipatsa dipo monga mphatso yopambana ina iliyonse. Kodi mphatso imeneyo ni ciyani? Ndipo tingacite ciyani poonetsa kuti timawayamikila cifukwa ca mphatso imeneyo?

1. Kodi njila imodzi yoyamikila zimene Mulungu na Khristu anaticitila ni iti?

Baibo imalonjeza kuti “aliyense wokhulupilila [Yesu]” angapeze moyo wosatha. (Yohane 3:16) Kodi mawu akuti ‘kukhulupilila’ atanthauza ciyani? Atanthauza kucita zambili kuposa kungokhulupilila cabe mwa Yesu. Timaonetsa cikhulupililo mwa zisankho zimene timapanga, komanso mwa zimene timacita. (Yakobo 2:17) Tikamaonetsa cikhulupililo cathu mwa zocita na zokamba zathu, timalimbitsa ubwenzi wathu na Yesu, komanso Atate wake Yehova.—Ŵelengani Yohane 14:21.

2. N’cocitika capadela citi cimene cimatipatsa mwayi woyamikila zimene Yehova na Yesu anaticitila?

Madzulo pa tsiku limene Yesu anaphedwa, iye anaonetsa otsatila ake njila ina yoyamikila nsembe yake. Anayambitsa mwambo wapadela umene Baibo imaucha “cakudya camadzulo ca Ambuye,” kapena kuti Mgonelo wa Ambuye, wodziŵikanso kuti Cikumbutso ca imfa ya Khristu. (1 Akorinto 11:20) Yesu anakhazikitsa mwambo umenewu na colinga cakuti atumwi ake, komanso Akhristu onse oona obwela pambuyo pawo, tizikumbukila kuti Yesu anapeleka moyo wake kaamba ka ife. Pa mwambo umenewu, Yesu analamulanso kuti: “Muzicita zimenezi pondikumbukila.” (Luka 22:19) Mukapezeka pa Cikumbutso, mumaonetsa kuyamikila cikondi cacikulu cimene Yehova na Yesu anationetsa.

KUMBANI MOZAMILAPO

Pezani njila zina zoyamikila cikondi cacikulu cimene Yehova na Yesu anationetsa. Ganizilani za kufunika kwa Cikumbutso ca imfa ya Khristu.

3. Kuyamikila kumatilimbikitsa kucitapo kanthu

Yelekezani kuti munali kumila pamadzi, ndiye munthu wina wakupulumutsani. Kodi mudzangocokapo n’kuiŵalako zimene munthuyo wakucitilani? Kapena mungapeze njila zomuyamikila pa zimene iye wakucitilani?

Tidzapeza moyo wosatha cifukwa ca cisomo ca Yehova. Ŵelengani 1 Yohane 4:8-10, na kukambilana mafunso aya:

  • N’cifukwa ciyani nsembe ya Yesu ni mphatso yapadela kwambili?

  • Kodi mumamva bwanji pa zimene Yehova na Yesu anakucitilani?

Kodi tingayamikile motani zimene Yehova na Yesu anaticitila? Ŵelengani 2 Akorinto 5:15, komanso 1 Yohane 4:11; 5:3. Pambuyo poŵelenga iliyonse ya Malemba awiliwa, kambilanani funso ili:

  • Malinga na lembali, tiyenela kucita ciyani kuti tionetse kuyamikila kwathu?

4. Tengelani citsanzo ca Yesu

Njila ina imene tingaonetsele kuyamikila kwathu ni kutengela citsanzo ca Yesu. Ŵelengani 1 Petulo 2:21, na kukambilana funso ili:

  • Ni njila ziti zimene tingatsatilile mapazi a Yesu mosamalitsa?

Yesu akuŵelenga Mawu a Mulungu mu mpukutu. Yesu akulankhula na mkazi wacisamariya pacitsime. Yesu akucilitsa munthu wodwala.

Yesu anali kukonda Mawu a Mulungu, anali kulalikila uthenga wabwino, ndiponso anali kuthandiza anthu

5. Muzipezeka pa Cikumbutso ca imfa ya Khristu

Kuti muone mmene unacitikila Mgonelo woyamba wa Ambuye, ŵelengani Luka 22:14, 19, 20. Ndiyeno kambilanani mafunso aya:

  • Kodi Mgonelo wa Ambuye unacitika motani?

  • Kodi mkate na vinyo ziimila ciyani?—Onani mavesi 19 na 20.

Yesu anafuna kuti otsatila ake azikumbukila imfa yake kamodzi pa caka, pa tsiku limene iye anaphedwa. Motelo, a Mboni za Yehova amasonkhana pamodzi caka ciliconse kuti akumbukile imfa ya Yesu m’njila imene iye analamula. Kuti mudziŵe zambili za msonkhano wofunika umenewu, Tambani VIDIYO. Ndiyeno kambilanani funso lotsatila.

VIDIYO: Kukumbukila Imfa ya Yesu (1:41)

Cocitika ca mu vidiyo yakuti ‘Kukumbukila Imfa ya Yesu.’ Mboni za Yehova zasonkhana pa Mgonelo wa Ambuye.
  • Kodi n’ciyani cimacitika pa Cikumbutso?

Mbale ya mkate wopanga cofufumitsa na tambula ya vinyo.

Mkate na vinyo ni zophiphilitsa cabe. Mkate umaimila thupi la Yesu langwilo limene anapeleka kaamba ka ife. Vinyo amaimila magazi ake

Akupatsilana vinyo pa Mgonelo wa Ambuye.

ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI: “Ine n’namulandila kale Yesu monga mpulumutsi wanga, conco sinifunikilanso kucita ciliconse.”

  • Kodi mungaseŵenzetse bwanji Yohane 3:16 na Yakobo 2:17, poonetsa kuti palinso zina zofunikila kucita?

CIDULE CAKE

Timayamikila zimene Yesu anaticitila poonetsa cikhulupililo mwa iye, komanso kupezeka pa Cikumbutso ca imfa yake.

Mafunso Obweleza

  • Kodi kuonetsa cikhulupililo mwa Yesu kumatanthauza ciyani?

  • Kodi mungayamikile bwanji zimene Yehova na Yesu anakucitilani?

  • N’cifukwa ciyani ni cinthu cofunika kwambili kupezeka pa Cikumbutso ca imfa ya Khristu?

Colinga

FUFUZANI

Kodi imfa ya Khristu imatilimbikitsa kucita ciyani?

Anagwiritsa Ntchito Thupi Lake Polemekeza Yehova (9:28)

Dziŵani zambili zokhudza cikhulupililo na mmene tingacionetsele.

“Khalani na Cikhulupililo m’Malonjezo a Yehova” (Nsanja ya Mlonda, October 2016)

Mu nkhani yakuti “Nikuona Kuti Ndine Woyela Komanso Nili na Moyo Waphindu,” onani mmene mayi wina anapindulila pa umoyo wake atamvetsetsa za nsembe ya Khristu.

“Baibo Imasintha Anthu” (Nsanja ya Mlonda, August 1, 2011)

Onani cifukwa cake ni anthu ocepa cabe amene amadyako kapena kumwako ziphiphilitso pa Cikumbutso.

“N’chifukwa Chiyani a Mboni za Yehova Mumachita Mwambo wa Mgonero wa Ambuye Mosiyana ndi Zipembedzo Zina?” (Nkhani ya pawebusaiti)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani