LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • “Lilani Ndi Anthu Amene Akulila”
    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila)—2017 | July
    • 14. Kodi anthu amene afedwa tingawatonthoze bwanji?

      14 M’pomveka kuti nthawi zina munthu amasoŵa cokamba kwa munthu amene ali na cisoni cacikulu. Ngakhale n’conco, Baibo imakamba kuti “lilime la anthu anzelu limacilitsa.” (Miy. 12:18) Pofuna kutonthoza ena, ambili apeza mfundo zolimbikitsa m’kabuku kakuti, Pamene Munthu Amene Mumakonda Amwalira.c Komabe, nthawi zambili cimene cimakhala cothandiza kwambili ndi ‘kulila ndi anthu amene akulila.’ (Aroma 12:15) Gaby, amene mwamuna wake anamwalila, anati: “Kulila n’kumene kumanitonthoza. N’cifukwa cake nimalimbikitsidwa ngati anzanga akulila nane. Panthawiyi, nimatonthozedwa poona kuti anzanga nawonso ali na cisoni.”

  • “Lilani Ndi Anthu Amene Akulila”
    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila)—2017 | July
    • 20. Kodi malonjezo a Yehova amatitonthoza bwanji?

      20 N’zolimbikitsa ngako kudziŵa kuti Yehova, Mulungu amene amatitonthoza m’njila iliyonse, adzathetsa cisoni conse. Adzacita zimenezi pamene “onse ali m’manda acikumbutso adzamva mau ake [a Yesu] ndipo adzatuluka.” (Yoh. 5:28, 29) Mulungu walonjeza kuti “adzameza imfa kwamuyaya ndipo Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, adzapukuta misozi pankhope zonse za anthu.” (Yes. 25:8) Panthawiyo, m’malo ‘molila ndi anthu amene akulila,’ tidzayamba ‘kusangalala ndi anthu amene akusangalala.’—Aroma 12:15.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani