LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 May tsa. 8
  • Khalani Monga Yosefe—Thaŵani Zaciwelewele

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Khalani Monga Yosefe—Thaŵani Zaciwelewele
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • “Thaŵani Dama”
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Kodi Baibo Imati Ciyani pa Nkhani ya Kugonana?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • “Thaŵani Dama”
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
  • Yehova Akukuthandizani Kupambana Mayeso
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 May tsa. 8
Yosefe akuthawa mkazi wa Potifara amene wagwila covala cake m’dzanja lake.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Khalani Monga Yosefe—Thaŵani Zaciwelewele

Yosefe anatipatsa citsanzo cabwino cimene tingatengele tikayesedwa kuti ticite zaciwelewele. Nthawi iliyonse pamene mkazi wa mbuye wake anamunyengelela kuti agone naye, iye anali kukana. (Gen. 39:7-10) Iye anali kuyankha kuti: “Ndingacitilenji coipa cacikulu conci n’kucimwila Mulungu?” Zimenezi zinaonetsa kuti anali ataganizilapo kale za mmene Yehova amaonela nkhani yokhala wokhulupilika m’cikwati. Ndiyeno pamene ciyeso cinakula, iye anathaŵa m’malo mozengeleza na kulola mkaziyo kumugonjetsa.—Gen. 39:12; 1 Akor. 6:18.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI THAWANI ZACIWELEWELE, PAMBUYO PAKE, YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Mee-Kyong akamba na Jin kusukulu.

    Kodi Jin anakumana na ciyeso canji?

  • Jin ayang’ana Mee-Kyong pamene aganizila pempho lake.

    Ni funso lofunika liti limene Jin anadzifunsa pamene Mee-Kyong anam’pempha kumuthandiza masamu kunyumba?

  • Kodi pempho la Mee-Kyong linam’khudza bwanji Jin?

  • Jin akamba na amalume ake amene ni mkulu.

    Kodi Jin anapeza bwanji thandizo?

  • Jin akana pempho lakuti akhale mnzake wa Mee-Kyong limene am’tumizila pa foni.

    Kodi Jin anacita ciani kuti athawe ciwelewele?

  • Kodi mwaphunzila ciani m’vidiyo imeneyi?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani