LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lff phunzilo 26
  • Kodi Zoipa Komanso Mavuto Zinakhalako Bwanji?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Zoipa Komanso Mavuto Zinakhalako Bwanji?
  • Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • KUMBANI MOZAMILAPO
  • CIDULE CAKE
  • FUFUZANI
  • N’cifukwa Ciani Pa Dziko Pali Mavuto Ambili Conco?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • N’cifukwa Ciani Mulungu Amalolela Kuti Anthu Azivutika?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • N’cifukwa Ciani Mulungu Amalolela Kuti Anthu Azivutika?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kodi Cifunilo ca Mulungu Kwa Anthu N’ciani?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
Onaninso Zina
Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
lff phunzilo 26
Phunzilo 26. Makolo a nkhawa akuona mwana wawo m’cipatala amene anapezeka mu ngozi.

PHUNZILO 26

Kodi Zoipa Komanso Mavuto Zinakhalako Bwanji?

Yopulinta
Yopulinta
Yopulinta

Coipa cikacitika, mwacibadwa timafunsa kuti, “N’cifukwa ciyani zacitika?” Koma ubwino wake ni wakuti, Baibo imapeleka yankho lomveka bwino pa funso limeneli.

1. Kodi Satana anaziyambitsa bwanji zinthu zoipa padziko?

Satana Mdyelekezi anapandukila Mulungu. Pofuna ulamulilo, Satana ananyengelela anthu oyambawo, Adamu na Hava, kuti agwilizane naye pa kupanduka kwake. Satana anacita izi mwa kuuza Hava bodza. (Genesis 3:1-5) Iye anapangitsa Hava kuganiza kuti Yehova anali kum’mana cinacake cabwino. Cimene Satana anatanthauza n’cakuti anthu akhoza kupeza cimwemwe cacikulu ngati angaleke kumvela Mulungu. Iye ananama bodza loyamba pouza Hava kuti sadzafa. Pa cifukwa cimeneci, Baibo imachula Satana “kuti wabodza komanso tate wake wa bodza.”—Yohane 8:44.

2. Kodi Adamu na Hava anasankhapo kucita ciyani?

Yehova anali wowolowa manja kwambili kwa Adamu na Hava. Iye anawalola kudya zipatso za mtengo uliwonse m’munda wa Edeni kupatulapo mtengo umodzi wokha basi. (Genesis 2:15-17) Koma iwo anasankhabe kudya zipatso za mtengo woletsedwa umenewo. Conco Hava “anathyola cipatso ca mtengowo n’kudya.” Pambuyo pake, Adamu “nayenso anadya” (Genesis 3:6) Onse aŵili anapandukila Mulungu. Adamu na Hava pokhala angwilo, iwo analibe cikhotelelo cofuna kucita zoipa. Conco pamene anapandukila Mulungu, anacita kupanga cisankho cakuti asamumvele. Mwa kutelo, iwo anacimwa na kukana ulamulilo wa Mulungu. Cisankho cimeneco cinawabweletsela mavuto aakulu.—Genesis 3:16-19.

3. Kodi cisankho ca Adamu na Hava cinatikhudza motani?

Adamu na Hava atacimwa, anakhala opanda ungwilo. Mwa kutelo, anapatsila mbadwa zawo zonse kupanda ungwilo kwawo. Kunena za Adamu, Baibo imanena kuti: ‘Ucimo unaloŵa m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzela mwa ucimo, imfayo n’kufalikila kwa anthu onse.’—Aroma 5:12.

Anthufe timakumana na mavuto pa zifukwa zosiyana-siyana. Nthawi zina timagwela m’mavuto cifukwa ca zosankha zathu zosaganiza bwino. Nthawi zinanso timakumana na mavuto cifukwa ca zosankha zoipa za anthu ena. Koma nthawi zina timapezeka m’mavuto cifukwa ca tsoka basi.—Ŵelengani Mlaliki 9:11.

KUMBANI MOZAMILAPO

Onani cifukwa cake si Mulungu amene amacititsa zoipa kapena mavuto padziko lapansi, komanso mmene iye amamvela tikamavutika.

4. Amene anacititsa kuti tizikumana na mavuto

Anthu ambili amakhulupilila kuti Mulungu ni amene amalamulila dziko lapansi. Kodi zimenezi n’zoona? Tambani VIDIYO.

VIDIYO: Ndani Akulamulila Dziko? (1:24)

Ŵelengani Yakobo 1:13, komanso 1 Yohane 5:19, kenako kambilanani funso ili:

  • Kodi Mulungu ndiye amacititsa mavuto komanso zoipa?

5. Onani zotulukapo za ulamulilo wa Satana

Tambani VIDIYO.

VIDIYO: N’cifukwa Ciani Mulungu Amalola Kuti Anthu Azivutika?—Mbali Yake (3:07)

Ŵelengani Genesis 3:1-6, na kukambilana mafunso aya:

  • Kodi Satana anakamba bodza lakuti ciyani?—Onani vesi 4 na 5.

  • Mwa zimene Satana anakamba, kodi anatanthauza bwanji kuti Yehova anafuna kumana anthu cinacake cabwino?

  • Malinga n’kunena kwa Satana, kodi iye amaona kuti anthu amafunikila Ulamulilo wa Yehova kuti akhale acimwemwe?

Ŵelengani Mlaliki 8:9, na kukambilana funso ili:

  • Cifukwa Yehova si ndiye akulamulila dzikoli, kodi cacitika n’ciyani?

Zithunzi zofotokoza mmene dziko lapansi lakhalila kucokela pa kulengedwa mpaka m’paradaiso wa kutsogolo. A. Paradaiso wobiliŵila bwino padziko lapansi. B. Maulamulilo a anthu padziko lapansi kwa zaka mazana ambili, odzala na zipembedzo zonyenga, magaŵano, nkhondo, na kuwononga za cilengedwe. Maboma ena amphamvu oonetsedwa pa cithunzi ndiwo Iguputo, China, Greece, Roma, Great Britain, komanso America. C. Anthu m’dziko lapansi lokozedwanso la Paradaiso.
  1. Adamu na Hava anali anthu angwilo m’Paradaiso. Koma cifukwa comvela zokamba za Satana, iwo anapandukila Yehova

  2. Pambuyo pa cipanduko cimeneco, padziko lapansi panadzala macimo, mavuto, komanso imfa

  3. Yehova adzacotsapo macimo, mavuto onse, ngakhale imfa. Pa nthawi imeneyo, anthu adzakhalanso angwilo m’Paradaiso

6.Yehova amatidela nkhawa tikakhala pa mavuto

Kodi n’zoona kuti Mulungu amatidela nkhawa tikakhala pa mavuto? Onani zimene Mfumu Davide komanso mtumwi Petulo analemba. Ŵelengani Salimo 31:7, komanso 1 Petulo 5:7, na kukambilana funso ili:

  • Kodi mukumva bwanji podziŵa kuti tikakhala pa mavuto, Yehova amaona komanso amatidela nkhawa?

7. Mulungu adzacotsapo mavuto onse amene timakumana nawo

Ŵelengani Yesaya 65:17, komanso Chivumbulutso 21:3, 4, na kukambilana funso ili:

  • N’cifukwa ciyani n’zokhazika mtima pansi kudziŵa kuti Yehova adzacotsapo mavuto onse amene anthu amakumana nawo?

Kodi mudziŵa?

Pamene Satana anakamba bodza loyamba, ananenela Yehova misece. Kutanthauza kuti anawononga mbili ya Yehova monga Wolamulila wolungama komanso wacikondi. Posacedwa, Yehova akadzacotsapo mavuto onse amene anthu amakumana nawo. Adzacotsanso citonzo pa dzina lake. Kunena kwina, iye adzatitsimikizila kuti ulamulilo wake ndiwo wabwino kopambana. Kuyeletsedwa kwa dzina la Yehova ndiyo nkhani yofunika kopambana m’cilengedwe conse.—Mateyu 6:9, 10.

ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI: “Mavuto amene amatigwela, ni Mulungu amene anakonzelatu.”

  • Nanga inu muona bwanji?

CIDULE CAKE

Satana Mdyelekezi komanso anthu aŵili oyambilila ndiwo anayambitsa zoipa padziko lapansi. Yehova zimamukhudza kwambili pamene tikukumana na mavuto, n’cifukwa cake adzawacotsapo posacedwa.

Mafunso Obweleza

  • Kodi Satana Mdyelekezi anauza Hava bodza lakuti ciyani?

  • Kodi kupanduka kwa Adamu na Hava kunatikhudza bwanji ife tonse?

  • Tidziŵa bwanji kuti Yehova amatidela nkhawa tikamakumana na mavuto?

Colinga

FUFUZANI

Dziŵani tanthauzo la m’Baibo la ucimo.

“Kodi Tchimo N’chiyani?” (Nkhani ya pawebusaiti)

Ŵelengani zowonjezela zokhudza nkhani imene Satana Mdyelekezi anayambitsa m’munda wa Edeni.

“N’cifukwa Ciyani Mulungu Amalola Kuti Anthufe Tizivutika?” (Nsanja ya Mlonda, January 1, 2014)

Mvetsetsani mayankho okhazika mtima pansi pa funso lovuta ili.

“N’chifukwa Chiyani Mulungu Analola Kuti Anthu Ambirimbiri Aphedwe mu Ulamuliro wa Nazi ku Germany?” (Nkhani ya pawebusaiti)

Onani zimene munthu wina anaphunzila cifukwa coona mavuto ambili.

Sinilinso Nekha Lomba (5:09)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani