LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 6/14 tsa. 7
  • Kubweleza za M’sukulu ya Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kubweleza za M’sukulu ya Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 6/14 tsa. 7

Kubweleza za M’sukulu ya Ulaliki

Tidzakambilana mafunso otsatilawa pa Sukulu ya Ulaliki mkati mwa mlungu wa June 30, 2014.

Taonetsa deti la mlungu umene tidzaphunzila mfundo iliyonse. Tacita zimenezi kuti mlungu uliwonse tizifufuza mfundozo pokonzekela.

  1. N’cifukwa ciani mfundo ya pa Ekisodo 23:2 ndi yofunika kwambili posankha zosangulutsa? [May 5, w11 7/15 mas. 10 mpaka 11 ndime 3-7]

  2. Kodi lamulo lakuti ansembe azisamba popeleka nsembe kwa Yehova linali lofunika motani? Nanga masiku ano lamulo limeneli litikumbutsa ciani monga atumiki a Mulungu? (Eks. 30:18-21) [May 19, w96 7/1 tsa. 9 ndime 9]

  3. N’cifukwa ciani Aroni sanalangidwe pamene anapanga mwana wa ng’ombe wagolide? (Eks. 32:1-8, 25-35) [May 19, w04 3/15 tsa. 27 ndime 4]

  4. Kodi lamulo la Mulungu kwa Aisiraeli loletsa kukwatilana ndi mitundu ina limafanana bwanji ndi mmene Mkristu amaonela cisumbali ndi cikwati? (Eks. 34:12-16) [May 26, w89 11/1 mas. 20-21 ndime 11-13]

  5. N’cifukwa ciani zocitika paumoyo wa Bezaleli ndi Oholiabu n’zolimbikitsa kwa ife? (Eks. 35:30-35) [May 26, w10 9/15 tsa. 10 ndime 13]

  6. “Cizindikilo copatulika ca kudzipeleka” pa nduwila imene mkulu wansembe anali kuvala ndi cikumbutso ca n’ciani? Nanga cizindikilo cimeneci cimatikumbutsa ciani pa kudzipeleka kwathu? (Eks. 39:30) [June 2, w01 2/1 tsa. 14 ndime 2-3]

  7. Kodi Akristu onse ali ndi udindo wotani ponena za kuulula macimo aakulu amene Mkristu wina wacita? (Lev. 5:1) [June  9, w97 8/15 tsa. 27]

  8. M’nthawi ya Aisiraeli kodi nsembe zacinyanjo zinali zofunika motani? Nanga zili ndi tanthauzo lanji kwa ife masiku ano? (Lev. 7:31-33) [June 16, w12 1/15 tsa. 19 ndime 11-12]

  9. Kodi chimo la ana a Aroni, Nadabu ndi Abihu, lingakhale kuti linaphatikizapo ciani? Nanga nkhani imeneyi itiphunzitsa ciani? (Lev.  10:1, 2,  9) [June 23, w04 5/15 tsa. 22 ndime 6-8]

  10. N’cifukwa ciani mkazi anali kukhala “wodetsedwa” akabeleka mwana? (Lev. 12:2, 5) [June 23, w04 5/15 tsa. 23 ndime 2]

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani