Yobu
24 “Nʼchifukwa chiyani Wamphamvuyonse sanakhazikitse nthawi yachiweruzo?+
Nʼchifukwa chiyani anthu amene amamudziwa sanaone tsiku lake lachiweruzo?
2 Anthu amasuntha zizindikiro za malire.+
Iwo amaba ziweto nʼkuzipititsa pamalo awo odyetsera ziweto.
3 Amathamangitsa bulu wa ana amasiye
Ndipo amalanda ngʼombe yamphongo ya mkazi wamasiye kuti ikhale chikole.+
4 Amachititsa kuti osauka athawe mumsewu.
Anthu ovutika apadziko lapansi amabisala akawaona.+
5 Osaukawo amafunafuna chakudya ngati abulu+ amʼchipululu,
Amafunafuna chakudya cha ana awo mʼchipululu.
6 Amakolola mʼmunda mwa munthu wina
Ndipo amakunkha mʼmunda wa mpesa wa munthu woipa.
7 Osaukawo amakhala usiku wonse ali maliseche,+
Amakhala pamphepo opanda chofunda.
8 Amanyowa ndi mvula mʼmapiri,
Ndipo amakhala pafupi ndi matanthwe chifukwa chakuti alibe pobisala.
9 Oipa amalanda mwana wamasiye kumʼchotsa pabere.+
Ndipo amatenga zovala za osauka kuti zikhale chikole,+
10 Moti amakakamizika kuyenda maliseche,
Komanso amasenza mitolo ya tirigu ali ndi njala.
11 Osaukawo amagwira ntchito mwakhama mʼmigula* ya mʼminda dzuwa likuswa mtengo.*
Amaponda mphesa koma amakhala ndi ludzu.+
12 Anthu amene akufa amakhala akubuula mumzinda.
Anthu amene avulala koopsa amapempha* thandizo,+
Koma Mulungu saona zimenezi ngati zolakwika.*
14 Munthu wopha anthu amadzuka mʼmamawa.
Iye amapha anthu ovutika komanso osauka,+
Ndipo usiku amakhala wakuba.
Ndipo amaphimba nkhope yake.
16 Mumdima anthu oipawo amathyola nyumba za anthu,
Masana amadzitsekera mʼnyumba.
Iwo amadana ndi kuwala.+
17 Kwa iwo mʼmawa nʼchimodzimodzi ndi mdima wandiweyani,
Amadziwa zoopsa zamumdima wandiweyani.
18 Koma iwo amatengedwa mwamsanga ndi madzi.
Malo awo adzakhala otembereredwa.+
Sadzabwerera kuminda yawo ya mpesa.
19 Mofanana ndi madzi amunthaka* amene amauma mʼnyengo yachilimwe komanso kunja kukatentha,
20 Mayi ake adzamuiwala* ndipo mphutsi zidzamudya.
Iye sadzakumbukiridwanso.+
Ndipo kupanda chilungamo kudzathyoledwa ngati mtengo.
21 Iye amachitira zoipa mkazi wosabereka,
Komanso amachitira nkhanza mkazi wamasiye.
22 Mulungu adzagwiritsa ntchito mphamvu zake powononga anthu amphamvu.
Ngakhale atakhala ndi mphamvu, iwo sadziwa ngati angakhalebe ndi moyo kapena ayi.
23 Mulungu amawalola kuti azidzidalira komanso kuti akhale otetezeka.+
24 Oipawo amakhala okwezeka kwa kanthawi, kenako nʼkutha.+
Iwo ali ngati ngala za tirigu zimene zimadulidwa nʼkuikidwa pamodzi.
Amatsitsidwa+ ndipo amafa mofanana ndi anthu ena onse.
25 Choncho ndi ndani amene angapereke umboni wosonyeza kuti ndine wabodza
Kapena kutsutsa mawu angawa?”