Yobu
36 Elihu anapitiriza kunena kuti:
2 “Ndilezereni mtima kwa kanthawi kochepa kuti ndifotokoze,
Chifukwa ndidakali ndi mawu oti ndinene mʼmalo mwa Mulungu.
3 Ndifotokoza mwatsatanetsatane zimene ndikudziwa,
Ndipo ndinena kuti amene anandipanga, ndi wachilungamo.+
4 Ndikunena zoona, mawu anga si onama.
Amene amadziwa chilichonse+ akukuonani.
5 Inde, Mulungu ndi wamphamvu+ ndipo sakana munthu aliyense.
Iye ali ndi mphamvu zazikulu zomvetsa zinthu.*
7 Iye sasiya kuyangʼanitsitsa wolungama.+
Amawaika kukhala mafumu,+ ndipo amalemekezeka mpaka kalekale.
8 Koma akamangidwa mʼmatangadza,
Nʼkugwidwa ndi zingwe zamavuto,
9 Iye amawaululira zimene achita,
Zimene alakwitsa chifukwa cha kunyada kwawo.
10 Iye amatsegula makutu awo kuti awapatse malangizo
Ndi kuwauza kuti asiye kuchita zoipa.+
11 Akamamumvera komanso kumutumikira,
Zinthu zidzawayendera bwino pa nthawi yonse ya moyo wawo,
Ndipo moyo wawo udzakhala wosangalatsa.+
13 Anthu oipa mtima* adzasunga chakukhosi.
Iwo sapempha thandizo ngakhale Mulungu atawamanga.
15 Koma Mulungu amapulumutsa anthu ovutika pa mavuto awo,
Amatsegula makutu awo akamaponderezedwa.
16 Iye amakukokani mukatsala pangʼono kukumana ndi mavuto+
Nʼkukupititsani pamalo otakasuka, opanda mavuto.+
Patebulo panu pali chakudya chambiri chabwino chimene chimakusangalatsani.+
17 Kenako mudzakhutira ndi chiweruzo chimene chidzaperekedwe kwa oipa.+
Pa nthawi imene chiweruzo chidzaperekedwe komanso chilungamo chidzatsatiridwe.
18 Samalani kuti mkwiyo usakuchititseni zinthu mwanjiru,*+
Ndipo musalole kuti akupatseni ziphuphu zambiri nʼkukusocheretsani.
19 Kodi kulira kwanu kopempha thandizo
Kapena kuyesetsa kwanu mwamphamvu kungakuthandizeni kuti musakumane ndi mavuto?+
20 Musamalakelake kuti usiku ufike,
Pamene anthu amasowa pamalo awo.
21 Samalani kuti musayambe kuchita zinthu zoipa,
Musasankhe zimenezi mʼmalo mwa mavuto.+
22 Pajatu Mulungu ali ndi mphamvu zapamwamba.
Kodi pali mphunzitsi winanso wofanana naye?
23 Ndi ndani anauzapo Mulungu kuti chitani izi,+
Kapena ndi ndani amene anamuuza kuti, ‘Zimene mwachitazi ndi zolakwikaʼ?+
25 Anthu onse aziona,
Munthu amaziyangʼana ali patali.
26 Inde Mulungu ndi wamkulu kuposa mmene tikudziwira.+
27 Iye amakoka madontho a madzi.+
Madonthowo amasintha nʼkukhala nkhungu imene imapanga mvula,
28 Kenako mitambo imagwetsa mvula,+
Imagwetsera aliyense madzi.
29 Kodi alipo amene angamvetse mmene mitambo anaitambasulira,
31 Pogwiritsa ntchito zimenezi, iye amapereka chakudya kwa anthu onse.
Amawapatsa chakudya chochuluka.+
32 Iye amafumbata mphezi mʼmanja mwake,
Ndipo amailamula kuti ikagwere pamene akufuna.+
33 Mabingu ake amanena za iye,
Ngakhale ziweto zimadziwa amene akubwera.”