Yeremiya
12 Inu Yehova, ndikabweretsa dandaulo langa kwa inu,
Komanso ndikamalankhula ndi inu nkhani zokhudza chilungamo, mumasonyeza kuti ndinu wolungama.+
Koma nʼchifukwa chiyani anthu oipa, zinthu zikuwayendera bwino,+
Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu amene amachita zachinyengo amakhala opanda nkhawa?
2 Munawadzala ndipo iwo anazika mizu.
Akula ndipo abala zipatso.
Amakutchulani pafupipafupi, koma mtima wawo uli kutali* kwambiri ndi inu.+
3 Koma inu Yehova, mukundidziwa bwino+ ndipo mumandiona.
Mwafufuza mtima wanga ndipo mwapeza kuti ndine wokhulupirika kwa inu.+
Apatuleni ngati nkhosa zimene zikukaphedwa,
Ndipo muwaike padera poyembekezera tsiku limene adzaphedwe.
4 Kodi dzikoli likhalabe lofota mpaka liti?
Kodi zomera zamʼmunda uliwonse zikhalabe zouma mpaka liti?+
Chifukwa cha zinthu zoipa zimene anthu amʼdzikoli akuchita,
Zilombo zakutchire ndi mbalame zawonongedwa.
Chifukwa anthuwo akuti: “Iye sakuona zimene zidzatichitikire.”
5 Ngati ukutopa pothamanga ndi anthu oyenda pansi,
Ndiye ungapikisane bwanji ndi mahatchi?+
Ukhoza kuona kuti ndiwe wotetezeka mʼdziko lamtendere,
Koma kodi udzatani ukadzakhala mʼnkhalango zowirira zamʼmphepete mwa Yorodano?
6 Chifukwa ngakhale abale ako enieni, anthu a mʼnyumba ya bambo ako,
Akuchitira zinthu zachinyengo.+
Iwo akunenera zinthu zoipa mofuula.
Usawakhulupirire,
Ngakhale atamalankhula zinthu zabwino kwa iwe.
7 “Nyumba yanga ndaisiya.+ Ndasiya cholowa changa.+
Wokondedwa wanga ndamupereka mʼmanja mwa adani ake.+
8 Cholowa changa chakhala ngati mkango kwa ine munkhalango.
Wokondedwa wanga wandibangulira.
Nʼchifukwa chake ndadana naye.
9 Cholowa changa chili ngati mbalame yanthenga zamitundu yosiyanasiyana imene imadya nyama.
Mbalame zina zodya nyama zaizungulira nʼkuiukira.+
Bwerani, sonkhanani pamodzi inu nyama zonse zamʼtchire,
Bwerani kuti mudzadye.+
Malo omwe ndi cholowa changa chosiririka awasandutsa bwinja moti palibe aliyense amene akukhalamo.
11 Cholowa changacho chasanduka chipululu,
Dziko lonse lakhala bwinja,
Koma palibe aliyense amene zikumukhudza.+
12 Anthu owononga adutsa mʼnjira zonse zodutsidwadutsidwa zamʼchipululu,
Chifukwa lupanga la Yehova likuwononga anthu kuchokera kumalekezero a dziko kukafika kumalekezero ena a dziko.+
Ndipo palibe munthu aliyense amene ali pamtendere.
13 Afesa tirigu koma akolola minga.+
Agwira ntchito yotopetsa koma osapeza phindu lililonse.
Iwo adzachita manyazi ndi zokolola zawo
Chifukwa mkwiyo waukulu wa Yehova udzawayakira.”
14 Yehova wanena kuti: “Anthu onse oipa amene ndinayandikana nawo amene akukhudza cholowa chimene ndinapatsa anthu anga Aisiraeli kuti chikhale chawo,+ ndikuwazula mʼdziko lawo+ ndipo ndidzazula nyumba ya Yuda pakati pawo. 15 Koma ndikadzawazula, ndidzawachitiranso chifundo moti ndidzabwezeretsa aliyense wa iwo pacholowa chake ndi pamalo ake.
16 Ndiyeno anthu a mitundu ina akadzayesetsa kuphunzira njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa kuti, ‘Pali Yehova Mulungu wamoyo!’ ngati mmene iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, anthu a mitundu inawo adzakhazikika pakati pa anthu anga. 17 Koma akadzakana kumvera, ine ndidzazulanso anthu a mtundu umenewo. Ndidzawazula nʼkuwawononga,” akutero Yehova.+