-
Yesaya 20:3, 4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Kenako Yehova anati: “Mtumiki wanga Yesaya wayenda maliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu, kuti akhale chizindikiro+ ndi chenjezo kwa Iguputo+ ndi Itiyopiya.+ 4 Mofanana ndi zimenezi, mfumu ya Asuri idzagwira gulu la anthu ku Iguputo+ ndi ku Itiyopiya nʼkupita nawo ku ukapolo kudziko lina. Idzagwira anyamata ndi amuna achikulire, ali opanda zovala ndi opanda nsapato, ndiponso matako awo ali pamtunda moti Iguputo adzachititsidwa manyazi.
-
-
Ezekieli 30:4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Lupanga lidzabwera kudzaukira Iguputo, ndipo anthu a ku Itiyopiya adzachita mantha kwambiri anthu akadzaphedwa ku Iguputo.
Chuma cha Iguputo chidzalandidwa ndipo maziko ake adzagwetsedwa.+
-