Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Deuteronomo 28:52
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 52 Adzakuzungulirani nʼkukutsekerani mʼmizinda yanu* mʼdziko lanu lonse, mpaka mipanda yanu yaitali ndi yolimba kwambiri imene mukuidalira itagwa. Adzakuzungulirani ndithu mʼmizinda yanu yonse mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.+

  • 2 Mafumu 25:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Mʼchaka cha 9 cha ufumu wa Zedekiya, mʼmwezi wa 10, pa tsiku la 10 la mweziwo, Nebukadinezara+ mfumu ya Babulo anabwera ku Yerusalemu pamodzi ndi asilikali ake onse.+ Anabwera kudzamenyana ndi anthu amumzindawo ndipo anamanga msasa komanso mpanda kuzungulira mzinda wonsewo.+ 2 Mzindawo unazunguliridwa mpaka chaka cha 11 cha Mfumu Zedekiya.

  • Yesaya 29:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Ine ndidzamanga misasa mokuzungulira mbali zonse,

      Ndidzamanga mpanda wa mitengo yosongoka mokuzungulira,

      Ndipo ndidzamanga malo okwera omenyerapo nkhondo kuti ndimenyane nawe.+

  • Yeremiya 39:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 39 Mʼchaka cha 9 cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya ya Yuda, mʼmwezi wa 10, Mfumu Nebukadinezara* ya Babulo ndi asilikali ake onse anafika ku Yerusalemu nʼkuzungulira mzindawo.+

  • Ezekieli 4:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Iwe mwana wa munthu, tenga njerwa ndipo uiike patsogolo pako. Panjerwapo ujambulepo mzinda wa Yerusalemu. 2 Umenye nkhondo ndi mzindawo+ ndipo umange mpanda womenyerapo nkhondo kuzungulira mzinda wonsewo.+ Umangenso malo okwera omenyerapo nkhondo+ komanso misasa ya asilikali. Uikenso zida zankhondo zogumulira mpanda wa mzindawo kuzungulira mzinda wonsewo.+

  • Ezekieli 21:21, 22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Chifukwa mfumu ya Babulo idzaima pamalo pamene misewu iwiriyo yagawikana kuti iwombeze maula. Mfumuyo idzagwedeza mivi, idzafunsira kwa mafano ake* komanso idzawombeza maula pogwiritsa ntchito chiwindi cha nyama. 22 Maula amene adzakhale mʼdzanja lake lamanja, adzasonyeza kuti apite ku Yerusalemu, akaike zida zogumulira mzindawo, akalamule asilikali ake kuti aphe anthu, akalize chizindikiro cha nkhondo, akaike zida zogumulira mageti a mzindawo, akamange malo okwera omenyerapo nkhondo ndiponso kuti akamange mpanda womenyerapo nkhondo.+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani