Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mafumu 24:14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Mfumuyo inatenga anthu onse a ku Yerusalemu, akalonga onse,+ asilikali onse amphamvu, amisiri onse ndiponso anthu osula zitsulo*+ nʼkupita nawo ku Babulo. Anthu onse amene inawatenga analipo 10,000. Palibe amene anatsala, kupatulapo anthu osauka kwambiri a mʼdzikolo.+ 15 Choncho iye anatenga Yehoyakini+ nʼkupita naye ku Babulo.+ Ku Yerusalemu anatenganso mayi a mfumuyo, akazi ake, nduna za panyumba yake komanso akuluakulu a mʼdzikolo, nʼkupita nawo ku Babulo.

  • 2 Mbiri 36:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Chakumayambiriro kwa chaka, Mfumu Nebukadinezara inatuma asilikali ake omwe anakamutenga nʼkubwera naye ku Babulo+ limodzi ndi zinthu zabwino zamʼnyumba ya Yehova.+ Komanso Nebukadinezara anasankha Zedekiya, yemwe anali mʼbale wa bambo ake a Yehoyakini, kuti akhale mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.+

  • Yeremiya 24:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu amene anali patsogolo pa kachisi wa Yehova. Anandionetsa madenguwo pambuyo poti Nebukadinezara* mfumu ya Babulo watenga Yekoniya*+ mwana wa Yehoyakimu,+ mfumu ya Yuda, pamodzi ndi akalonga a Yuda, amisiri komanso anthu osula zitsulo,* kuchoka ku Yerusalemu nʼkupita nawo ku ukapolo ku Babulo.+

  • Danieli 1:2, 3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Kenako Yehova anapereka Mfumu Yehoyakimu ya Yuda mʼmanja mwake,+ limodzi ndi zina mwa ziwiya za mʼnyumba ya* Mulungu woona. Nebukadinezara anatenga ziwiyazo nʼkupita nazo kudziko la Sinara,*+ kunyumba* ya mulungu wake ndipo anakaziika mʼnyumba yosungiramo chuma ya mulungu wake.+

      3 Ndiyeno mfumu inalamula Asipenazi, mkulu wa nduna zapanyumba ya mfumu kuti abweretse ena mwa Aisiraeli,* kuphatikizapo a mʼbanja lachifumu komanso anthu olemekezeka.+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani