Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mafumu 25:13, 14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Akasidi anaphwanyaphwanya zipilala zakopa+ zomwe zinali mʼnyumba ya Yehova, zotengera zokhala ndi mawilo+ ndiponso thanki ya kopa yosungira madzi+ zimene zinali mʼnyumba ya Yehova, nʼkutenga kopa wake kupita naye ku Babulo.+ 14 Akasidiwo anatenganso ndowa, mafosholo, zozimitsira nyale, makapu ndi ziwiya zonse zakopa zimene ansembe ankagwiritsa ntchito potumikira mʼkachisi.

  • 2 Mbiri 36:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Mfumuyo inatenga ziwiya zonse, zazikulu ndi zazingʼono, zamʼnyumba ya Mulungu woona. Inatenganso chuma cha mʼnyumba ya Yehova, chuma cha mfumu ndi cha akalonga ake. Inatenga chilichonse nʼkupita nacho ku Babulo.+

  • Yeremiya 52:17, 18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Akasidi anaphwanyaphwanya zipilala zakopa+ zapanyumba ya Yehova, zotengera zokhala ndi mawilo+ ndiponso thanki yakopa yosungira madzi+ zimene zinali mʼnyumba ya Yehova nʼkutenga kopa yense kupita naye ku Babulo.+ 18 Akasidiwo anatenganso ndowa, mafosholo, zozimitsira nyale, mbale zolowa,+ makapu+ ndi ziwiya zonse zakopa zimene ansembe ankagwiritsa ntchito potumikira mʼkachisi.

  • Danieli 5:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ndiyeno anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼkachisi, mʼnyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Kenako mfumuyo, nduna zake, adzakazi ake ndi akazi ake ena anayamba kumwera mʼziwiyazo.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani