Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Lero

Lamlungu, November 2

Choncho tisapitirize kugona ngati mmene ena onse akuchitira, koma tikhalebe maso ndipo tikhalebe oganiza bwino.​—1 Ates. 5:6.

Chikondi n’chofunika kuti tikhalebe maso komanso tiziganiza bwino. (Mat. 22:37-39) Kukonda Mulungu kumatithandiza kuti tizipirira tikamagwira ntchito yolalikira ngakhale pamene kuchita zimenezi kungatibweretsere mavuto. (2 Tim. 1:7, 8) Chifukwa chokonda anthu omwe satumikira Yehova, timapitirizabe kulalikira ngakhalenso kudzera pafoni komanso polemba makalata. Sitifooka chifukwa timayembekezera kuti tsiku lina, anthu amenewa adzasintha n’kuyamba kuchita zinthu zabwino. (Ezek. 18:27, 28) Kukonda anthu kumaphatikizapo kukonda Akhristu anzathu. Timasonyeza chikondichi ‘potonthozana ndi kulimbikitsana.’ (1 Ates. 5:11) Mofanana ndi asilikali, omwe amathandizana pa nthawi ya nkhondo, ifenso timalimbikitsana. Sitingakhumudwitse mwadala abale ndi alongo athu kapenanso kuwabwezera zoipa. (1 Ates. 5:13, 15) Timasonyezanso chikondi polemekeza abale omwe amatsogolera mumpingo.—1 Ates. 5:12. w23.06 26:6, 10-11

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lolemba, November 3

[Yehova] akanena kanthu, kodi angalephere kuchita?​—Num. 23:19.

Njira imodzi yomwe tingalimbitsire chikhulupiriro chathu ndi kuganizira mozama zokhudza dipo. Dipo ndi lomwe limatitsimikizira kuti malonjezo a Mulungu adzakwaniritsidwa. Tikamaganizira mosamala chifukwa chake dipo linaperekedwa komanso zimene zinalowetsedwapo, timayamba kukhulupirira kwambiri kuti lonjezo la Mulungu loti tidzakhala ndi moyo wosatha m’dziko labwino lidzakwaniritsidwa. N’chifukwa chiyani tikutero? Kodi panafunika chiyani kuti dipo liperekedwe? Yehova anatumiza Mwana wake wokondedwa woyamba kubadwa komanso mnzake wapamtima, kuti adzabadwe monga munthu wangwiro padzikoli. Ali padzikoli, Yesu anapirira mavuto osiyanasiyana. Kenako anazunzidwa komanso kufa imfa yowawa. Apatu Yehova analipira mtengo wokwera kwambiri. Mulungu wathu wachikondi sakanalola kuti Mwana wake avutike n’kufa pongofuna kuti tidzakhale ndi moyo wabwino koma waufupi. (Yoh. 3:16; 1 Pet. 1:18, 19) Chifukwa choti anapereka mtengo wokwera chonchi, Yehova adzaonetsetsa kuti tidzakhale ndi moyo wosatha m’dziko latsopano. w23.04 19:8-9

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachiwiri, November 4

Iwe Imfa amene umabweretsa ululu woopsa, kodi mphamvu yako ili kuti?​—Hos. 13:14.

Kodi Yehova amafunitsitsa kudzaukitsa akufa? N’zosachita kufunsa. Iye anauzira anthu angapo kuti alembe m’Baibulo lonjezo lake lakuti adzaukitsa akufa. (Yes. 26:19; Chiv. 20:11-13) Yehova akalonjeza, nthawi zonse amakwaniritsa zomwe walonjezazo. (Yos. 23:14) Ndipotu iye ndi wofunitsitsa kudzaukitsa anthu amene anamwalira. Taganizirani zomwe Yobu analankhula. Iye sankakayikira kuti ngakhale atamwalira, Yehova adzalakalaka kumuonanso ali ndi moyo. (Yobu 14:14, 15) Yehova amafunitsitsanso kudzaukitsa atumiki ake onse amene anamwalira, kuti akhale athanzi komanso osangalala. Nanga bwanji za anthu mabiliyoni omwe anamwalira asanapeze mwayi wophunzira za Yehova? Mulungu wathu wachikondi amafunanso kudzawaukitsa. (Mac. 24:15) Iye amafuna kuti iwo akhale ndi mwayi wokhala anzake komanso kuti adzakhale ndi mwayi wokhala padzikoli mpaka kalekale.—Yoh. 3:16. w23.04 16:5-6

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani