Yesaya
33 Tsoka iwe amene ukulanda zinthu koma iweyo osalandidwa. Tsoka kwa iwe amene ukuchita zachinyengo pamene ena sanakuchitire zachinyengo.+ Ukadzangomaliza kulanda, nawenso udzalandidwa.+ Ukadzangomaliza kuchitira ena zachinyengo, iwonso adzakuchitira zachinyengo.+
2 Inu Yehova, tikomereni mtima.+ Ife tikudalira inu.+ Tilimbitseni ndi dzanja lanu+ m’mawa uliwonse.+ Mukhale chipulumutso chathu pa nthawi ya masautso.+ 3 Mitundu ya anthu yathawa itamva mkokomo wa mawu anu.+ Mitundu yamwazikana chifukwa chakuti inu mwanyamuka.+ 4 Zinthu zimene anthu inu munalanda+ ena zidzasonkhanitsidwa ngati mphemvu zikasonkhana pamodzi, ndiponso ngati chigulu cha dzombe chimene chikukhamukira kwa munthu.+ 5 Yehova adzakwezedwa pamwamba,+ pakuti amakhala pamalo apamwamba.+ Iye adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo.+ 6 M’masiku anu, kukhulupirika kudzabweretsa chipulumutso chachikulu.+ Nazonso nzeru, kudziwa zinthu,+ ndi kuopa Yehova,+ komwe ndiko chuma chake zidzabweretsa chipulumutso chachikulu.
7 Ndipotu anthu awo otchuka adzalira mofuula m’misewu. Amithenga a mtendere+ adzalira momvetsa chisoni. 8 Misewu ikuluikulu yawonongeka.+ Palibenso munthu woyenda m’njira.+ Iye waphwanya pangano+ ndipo wanyansidwa ndi mizinda.+ Sasamala za munthu aliyense.+ 9 Dzikolo likulira, lafota.+ Lebanoni wachita manyazi, wanyala.+ Sharoni+ wakhala ngati chipululu ndipo Basana ndi Karimeli akuyoyola masamba awo.+
10 Yehova wati: “Tsopano ndinyamuka,+ ndidzikweza.+ Tsopano ndidziika pamwamba.+ 11 Anthu inu muli ndi pakati pa udzu wouma+ ndipo mudzabereka mapesi. Mzimu wanu udzakunyeketsani+ ngati moto.+ 12 Mitundu ya anthu idzakhala ngati zotsala za laimu akatenthedwa. Iwo adzayaka ndi moto ngati minga zimene zasadzidwa.+ 13 Anthu inu amene muli kutali, imvani zimene ndikufuna kuchita.+ Inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga.+ 14 Mu Ziyoni, anthu ochimwa akuchita mantha.+ Opanduka akunjenjemera kwambiri.+ Akufunsa kuti: ‘Ndani wa ife angakhale pambali pa moto wowononga?+ Ndani wa ife angakhale pafupi ndi moto woyaka kwambiri wosatherapo?’+
15 “Pali munthu amene amayenda m’chilungamo nthawi zonse,+ amene amalankhula zowongoka,+ amene amakana kupeza phindu mwachinyengo,+ amene salola kuti manja ake alandire chiphuphu,+ amene amatseka makutu ake kuti asamve nkhani zokhudza kukhetsa magazi, ndiponso amene amatseka maso ake kuti asaone zoipa.+ 16 Iye ndi amene adzakhale pamalo apamwamba.+ Malo ake okhala adzakhala otetezeka m’matanthwe movuta kufikamo.+ Iye adzapatsidwa chakudya+ ndipo madzi ake sadzatha.”+
17 Maso ako adzaona kukongola kwa mfumu.+ Adzaona dziko lakutali.+ 18 Mtima wako udzalankhula motsitsa mawu+ za chinthu choopsa kuti: “Kodi mlembi ali kuti? Kodi wopereka malipiro uja ali kuti?+ Uja amawerenga nsanjayu ali kuti?”+ 19 Simudzaona anthu achipongwe, amene chilankhulo chawo n’chovuta kumva, anthu achibwibwi olankhula zinthu zovuta kumva.+ 20 Taonani Ziyoni,+ tauni yathu yochitiramo zikondwerero.+ Maso anu adzaona Yerusalemu, amene ndi malo okhala aphee, opanda chosokoneza chilichonse. Iye ndi hema woti palibe amene adzamuchotse.+ Zikhomo zake sizidzazulidwa ndipo zingwe zake sizidzaduka.+ 21 Koma kumeneko, Yehova Wolemekezeka+ adzakhala malo a mitsinje+ ndi a ngalande zikuluzikulu kwa ife. Kumalo amenewo sikudzadutsa gulu la ngalawa kapena zombo zikuluzikulu. 22 Pakuti Yehova ndiye Woweruza wathu.+ Yehova ndiye Wotipatsa Malamulo.+ Yehova ndiye Mfumu yathu.+ Iye adzatipulumutsa.+
23 Zingwe zidzakhala zosamanga. Mtengo wautali wa pangalawa sadzatha kuuimika mowongoka. Chinsalu chapangalawayo sadzatha kuchitambasula.
Pa nthawi imeneyo adzagawana zofunkha zambirimbiri. Ngakhale anthu olumala adzatenga nawo katundu wambiri wofunkha.+ 24 Palibe munthu wokhala m’dzikolo amene adzanene kuti: “Ndikudwala.”+ Anthu okhala mmenemo adzakhala amene machimo awo anakhululukidwa.+