8 Potsirizira pake, Yuda anauza Isiraeli bambo ake kuti: “M’perekeni kwa ine mnyamatayu+ kuti tinyamuke tizipita. Tipite kuti tikhalebe ndi moyo tisafe,+ inuyo ndi ife, limodzi ndi ana athu aang’onowa.+
32 Ine kapolo wanu ndinadzipereka kukhala chikole+ cha moyo wa mwanayu pamene ali kutali ndi bambo ake. Ndinalonjeza kuti, ‘Ndikadzalephera kubwera naye kwa inu, ndidzakhale wochimwa kwa inu bambo anga moyo wanga wonse.’+