Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 19:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Pamenepo Mose anakwera m’phirimo kukaonekera kwa Mulungu woona. Ndipo Yehova anayamba kumulankhula m’phirimo+ kuti: “Ukanene mawu awa kunyumba ya Yakobo, ana a Isiraeli kuti,

  • Ekisodo 25:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Mukapange chihema chopatulika ndi ziwiya zake mogwirizana ndendende ndi zonse zimene ndikukusonyeza.+

  • Ekisodo 27:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Upange bokosi lamatabwa losatseka pansi. Alipange mmene iye wakusonyezera m’phiri.+

  • Machitidwe 7:44
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 “Makolo athuwo anali ndi chihema cha umboni m’chipululu. Anachipanga potsatira malangizo amene Mulungu anapereka pamene anali kulankhula ndi Mose. Mulungu anauza Mose kuti apange chihemacho molingana ndi chithunzi chimene anachiona.+

  • Aheberi 8:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Koma amuna amenewo akuchita utumiki wopatulikawo m’chifaniziro+ ndi mu mthunzi+ wa zinthu zakumwamba. Izi zinaonekera mu lamulo limene Mulungu anapatsa Mose, atatsala pang’ono kumanga chihema.+ Lamulo lake linali lakuti:+ “Uonetsetse kuti wapanga zinthu zonse motsatira chitsanzo chimene wasonyezedwa m’phiri.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena