28“Koma iwe patula Aroni m’bale wako pamodzi ndi ana ake pakati pa ana a Isiraeli, ndipo Aroniyo+ atumikire monga wansembe wanga pamodzi ndi ana akewo,+ Nadabu, Abihu,+ Eleazara ndi Itamara.+
43 Aroni ndi ana ake azivala makabudula amenewa polowa m’chihema chokumanako kapena popita kuguwa lansembe kukatumikira pamalo oyera, kuti asapalamule mlandu ndi kufa. Limeneli ndi lamulo kwa iye ndi mbadwa zake mpaka kalekale.+