20 Yosefe anabereka Manase+ ndi Efuraimu*+ ku Iguputo. Anabereka anawa kwa mkazi wake Asenati+ mwana wa Potifera, yemwe anali wansembe wa mzinda wa Oni.
5 Tsopano ana awiri amene unabereka ku Iguputo kuno ine ndisanabwere, ndi ana anga.+ Efuraimu ndi Manase akhala ana anga monga alili Rubeni ndi Simiyoni.+
16Malire a gawo+ la ana a Yosefe+ anayambira kumtsinje wa Yorodano+ kufupi ndi Yeriko kukafika kumadzi a Yeriko chakum’mawa, mpaka kuchipululu chochokera ku Yeriko kukafika kudera lamapiri la Beteli.+