Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 6:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 “‘Tsopano lamulo la nsembe yambewu+ lili motere: Ana a Aroni azibweretsa nsembeyi pamaso pa Yehova patsogolo pa guwa lansembe.

  • Levitiko 7:37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Limeneli ndilo lamulo lokhudza nsembe yopsereza,+ nsembe yambewu,+ nsembe yamachimo,+ nsembe ya kupalamula,+ nyama yoperekedwa polonga munthu unsembe+ ndiponso nsembe yachiyanjano,+

  • Numeri 28:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Pang’ombe iliyonse yamphongo, muzipereka ufa wosalala wokwana magawo atatu mwa magawo 10 a muyezo wa efa, monga nsembe yake yambewu.+ Ufawo uzikhala wothira mafuta. Nkhosa yamphongo imodziyo+ muziipereka limodzi ndi nsembe yambewu ya ufa wosalala wokwana magawo awiri mwa magawo 10 a muyezo wa efa. Ufawo uzikhala wothira mafuta.

  • Numeri 29:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Muzipereka nsembe zimenezi kuwonjezera pa nsembe yopsereza+ ya mwezi ndi mwezi, limodzi ndi nsembe yake yambewu.+ Muzizipereka kuwonjezeranso pa nsembe yopsereza+ ya tsiku ndi tsiku, limodzi ndi nsembe yake yambewu,+ limodzinso ndi nsembe zachakumwa.+ Muzipereka nsembe zopserezazo malinga ndi dongosolo lake la nthawi zonse, monga nsembe zotentha ndi moto zopereka fungo lokhazika mtima pansi kwa Yehova.+

  • 1 Mbiri 21:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Koma Orinani anauza Davide kuti: “Ingotengani malowa akhale anu,+ ndipo mbuyanga mfumu chitani chilichonse chimene mukuona kuti n’chabwino. Taonani, ineyo ndipereka ng’ombe+ kuti zikhale nsembe zopsereza ndi chopunthira tirigu+ kuti chikhale nkhuni,+ ndiponso ndipereka tirigu kuti akhale nsembe yambewu. Ndikupereka zonsezi.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena