12 Sonkhanitsani anthu,+ amuna, akazi, ana ndi alendo okhala m’mizinda yanu, kuti amvetsere ndi kuphunzira,+ pakuti ayenera kuopa Yehova Mulungu wanu+ ndi kutsatira mosamala mawu onse a m’chilamulo ichi.
2 Choncho Ezara wansembe+ anabweretsa chilamulo pamaso pa mpingo+ wa amuna komanso akazi ndi ana onse amene akanatha kumvetsera ndi kuzindikira+ zimene zinali kunenedwa. Limeneli linali tsiku loyamba la mwezi wa 7.+