12 Koma pakati pa anthu okhala ku Yabesi-giliyadi+ anapeza atsikana 400, anamwali+ amene anali asanagonepo ndi mwamuna. Amenewa anawabweretsa ku msasa ku Silo,+ m’dziko la Kanani.
14 Choncho, Abenjaminiwo anabwerera pa nthawiyo. Ndipo anawapatsa akazi amene anawasunga ndi moyo pakati pa akazi a ku Yabesi-giliyadi,+ koma sanawapezere akazi okwanira.+