Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 10:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 “Pa tsiku lanu losangalala,+ pa nyengo ya zikondwerero zanu,+ ndi pa masiku oyambira miyezi,+ muziliza malipengawo popereka nsembe zanu zopsereza+ ndi zachiyanjano.+ Kuliza malipengawo kudzakhala chikumbutso kwa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”+

  • Numeri 28:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “‘Kumayambiriro kwa mwezi uliwonse, muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Nsembeyo izikhala ng’ombe ziwiri zazing’ono zamphongo, nkhosa imodzi yamphongo, ndi ana a nkhosa 7 amphongo opanda chilema. Mwana wa nkhosa aliyense azikhala wachaka chimodzi.+

  • 2 Mafumu 4:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Mwamuna wakeyo anam’funsa kuti: “N’chifukwa chiyani mukufuna kupitako lero? Lero si tsiku lokhala mwezi+ kapena pasabata.” Koma mayiyo anayankha kuti: “Palibe kanthu.”

  • 1 Mbiri 23:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Anali kutumikiranso nthawi iliyonse yopereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa masabata,+ pa masiku okhala mwezi,+ ndi pa nyengo za chikondwerero.+ Nthawi zonse anali kutumikira popereka nsembezo kwa Yehova, malinga ndi ziwerengero zake, komanso potsata lamulo lake.

  • 2 Mbiri 2:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 ine ndikumanga+ nyumba ya dzina+ la Yehova Mulungu wanga kuti ndiipatule+ ikhale yake. Ndikufuna kuti ndizifukiziramo mafuta onunkhira+ pamaso pake, ndi kuti nthawi zonse muzikhala mkate wosanjikiza.+ Ndiponso m’nyumbayo ndiziperekeramo nsembe zopsereza m’mawa ndi madzulo+ pa masabata,+ pa masiku okhala mwezi,+ ndi pa nyengo ya zikondwerero+ za Yehova Mulungu wathu. Zimenezi zizichitika mu Isiraeli mpaka kalekale.*+

  • Nehemiya 10:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Akazigwiritsire ntchito pokonza mkate wosanjikiza,+ nsembe yachikhalire yambewu,+ nsembe yachikhalire yopsereza ya pa tsiku la sabata+ ndi tsiku lokhala mwezi.+ Akazigwiritsirenso ntchito pokonza madyerero a pa nthawi yoikidwiratu,+ zinthu zopatulika+ ndi nsembe yamachimo+ yophimbira machimo a Isiraeli komanso pa ntchito zonse za panyumba ya Mulungu wathu.+

  • Akolose 2:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Choncho munthu asakuweruzeni+ pa nkhani ya kudya ndi kumwa+ kapena chikondwerero chinachake,+ kapenanso kusunga tsiku lokhala mwezi,+ ngakhalenso kusunga sabata,+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena