-
2 Mbiri 29:25Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
25 Pa nthawi imeneyi, Hezekiya anaika Alevi+ panyumba ya Yehova atanyamula zinganga,+ zoimbira za zingwe,+ ndi azeze.+ Iwo anali kutsatira ndondomeko yoimbira imene anaikhazikitsa Davide,+ Gadi+ yemwe anali wamasomphenya wa mfumu, ndi mneneri Natani,+ popeza ndondomekoyo inachokera kwa Yehova kudzera mwa aneneri ake.+
-
-
Ezara 3:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 Tsopano anthu amene anali kugwira ntchito yomanga nyumbayo anamaliza kumanga maziko+ a kachisi wa Yehova. Atatero, ansembe ovala zovala zaunsembe+ omwe ananyamula malipenga,+ ndiponso Alevi ana a Asafu+ omwe ananyamula zinganga,+ anaimirira kuti atamande Yehova motsatira dongosolo+ limene Davide mfumu ya Isiraeli anakhazikitsa.
-
-
Nehemiya 12:27Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
27 Ndiyeno mwambo wotsegulira+ mpanda wa Yerusalemu uli pafupi kuchitika, anthu anafunafuna Alevi m’malo awo onse ndi kubwera nawo ku Yerusalemu. Anachita izi kuti potsegulira mpandawo pakhale kusangalala ndi kuyamika+ Mulungu mwa kuimba nyimbo+ pogwiritsa ntchito zinganga, zoimbira za zingwe+ ndi azeze.+
-