19 Amene ali kolowera dzuwa adzayamba kuopa dzina la Yehova,+ ndipo amene ali kotulukira dzuwa adzaopa ulemerero wake.+ Pakuti iye adzabwera ngati mtsinje woyambitsa mavuto woyendetsedwa ndi mzimu wa Yehova.+
7 Kodi ndani amene sangakuopeni,+ inu Mfumu ya mitundu yonse?+ Inuyo ndinu woyenera kuopedwa, chifukwa chakuti pakati pa anzeru onse a m’mitundu ya anthu ndiponso pakati pa maufumu awo onse, palibiretu aliyense wofanana ndi inu.+