Yobu 11:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Kodi ungazindikire zinthu zozama za Mulungu,+Kapena kodi ungadziwe mapeto a kukula kwa Wamphamvuyonse? Yobu 26:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Komatu zimenezi ndi kambali kakang’ono chabe ka zochita zake,+Ndipo timangomva kunong’ona kwapansipansi kwa mawu ake.Koma kodi mabingu ake amphamvu, angawamvetse ndani?”+ Salimo 40:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 Inu Yehova Mulungu wanga, mwatichitira zinthu zambiri zodabwitsa,+Ndipo mumatiganizira.+Palibe angafanane ndi inu.+Ndikafuna kulankhula ndi kunena za zodabwitsazo,Zimachuluka kwambiri moti sindingathe kuzifotokoza.+ Mlaliki 8:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Ndinaona ntchito yonse ya Mulungu woona,+ ndipo ndinaona kuti anthu amalephera kudziwa ntchito imene yachitika padziko lapansi pano.+ Kaya anthu ayesetse bwanji kuifufuza, safika poidziwa.+ Ngakhale atanena kuti ali ndi nzeru zokwanira zodziwira zinthu,+ sangathe kuidziwa.+ Aroma 11:33 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 33 Ndithudi, madalitso amene Mulungu amapereka ndi ochuluka kwambiri.+ Nzeru+ zake n’zozama, ndiponso iye ndi wodziwa zinthu kwambiri.+ Ziweruzo zake ndi zosasanthulika,+ ndipo ndani angatulukire njira zake?
7 Kodi ungazindikire zinthu zozama za Mulungu,+Kapena kodi ungadziwe mapeto a kukula kwa Wamphamvuyonse?
14 Komatu zimenezi ndi kambali kakang’ono chabe ka zochita zake,+Ndipo timangomva kunong’ona kwapansipansi kwa mawu ake.Koma kodi mabingu ake amphamvu, angawamvetse ndani?”+
5 Inu Yehova Mulungu wanga, mwatichitira zinthu zambiri zodabwitsa,+Ndipo mumatiganizira.+Palibe angafanane ndi inu.+Ndikafuna kulankhula ndi kunena za zodabwitsazo,Zimachuluka kwambiri moti sindingathe kuzifotokoza.+
17 Ndinaona ntchito yonse ya Mulungu woona,+ ndipo ndinaona kuti anthu amalephera kudziwa ntchito imene yachitika padziko lapansi pano.+ Kaya anthu ayesetse bwanji kuifufuza, safika poidziwa.+ Ngakhale atanena kuti ali ndi nzeru zokwanira zodziwira zinthu,+ sangathe kuidziwa.+
33 Ndithudi, madalitso amene Mulungu amapereka ndi ochuluka kwambiri.+ Nzeru+ zake n’zozama, ndiponso iye ndi wodziwa zinthu kwambiri.+ Ziweruzo zake ndi zosasanthulika,+ ndipo ndani angatulukire njira zake?