20 M’tsiku limenelo, otsala a Isiraeli+ ndi opulumuka a nyumba ya Yakobo sadzadaliranso yemwe akuwamenya,+ koma ndi mtima wonse adzadalira Yehova, Woyera wa Isiraeli.+
33 Yehova wa makamu wanena kuti: “Ana a Isiraeli ndi ana a Yuda, onse akuponderezedwa. Anthu onse amene agwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina akuwakakamira+ ndipo sakuwalola kubwerera kwawo.+