16 “Bwerani pafupi ndi ine anthu inu. Mvetserani izi. Kuyambira pa chiyambi, ine sindinalankhulirepo m’malo obisika.+ Pamene zinthu zonenedwazo zinayamba kuchitika, ine ndinalipo.”
Tsopano Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, watumiza ine ndiponso watumiza mzimu wake.+