12 Inu ana a Isiraeli, monga momwe munthu amathyolera zipatso mumtengo n’kuzisonkhanitsa+ pamodzi chimodzi ndi chimodzi, Yehova adzakusonkhanitsani inu+ amene mwamwazikana m’dera loyambira ku Mtsinje*+ mpaka kukafika kuchigwa* cha Iguputo.+
11 Pamenepo ana a Yuda ndi ana a Isiraeli adzasonkhanitsidwa pamodzi ndipo adzakhala ogwirizana.+ Iwo adzadziikira mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka m’dzikolo,+ chifukwa tsikuli lidzakhala lofunika kwambiri kwa Yezereeli.*+
31 Iye adzatumiza angelo ake ndi kulira kwamphamvu kwa lipenga,+ ndipo adzasonkhanitsa osankhidwa ake+ kuchokera kumphepo zinayi,+ kuchokera kumalekezero a m’mlengalenga mpaka kumalekezero ena.