Deuteronomo 28:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 “Mukapanda kumvera mawu a Yehova Mulungu wanu ndi kuonetsetsa kuti mukutsatira malamulo ake onse ndi mfundo zake zimene ndikukupatsani lero, matemberero otsatirawa adzakugwerani ndi kukupezani:+ Deuteronomo 29:27 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 27 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira dziko limeneli mwa kulibweretsera matemberero onse olembedwa m’buku ili.+ Yoswa 23:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Mawu onse abwino amene Yehova Mulungu wanu analankhula akwaniritsidwa pa inu,+ momwemonso Yehova adzakwaniritsa pa inu mawu onse oipa, kufikira atakufafanizani kukuchotsani padziko labwinoli, limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.+ 2 Mafumu 23:27 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 27 Koma Yehova anati: “Yuda+ nayenso ndim’chotsa pamaso panga+ monga mmene ndinachotsera Isiraeli,+ ndipo ndithu ndidzakana ngakhale mzinda wa Yerusalemu umene ndinausankha, ndi nyumba imene ndinanena kuti, ‘Dzina langa lizikhala pamenepo.’”+ Yeremiya 15:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 “‘Ndidzawagwetsera masoka a mitundu inayi,’+ watero Yehova. ‘Ndidzawatumizira lupanga kuti liwaphe, agalu kuti akoke mitembo yawo, zolengedwa zouluka zam’mlengalenga+ ndi zilombo zakutchire kuti ziwadye ndi kuwawononga. Mika 3:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Chotero Ziyoni adzagawulidwa ngati munda chifukwa cha anthu inu ndipo Yerusalemu adzangokhala milu ya mabwinja.+ Phiri la nyumba ya Mulungu lidzakhala ngati zitunda za m’nkhalango.
15 “Mukapanda kumvera mawu a Yehova Mulungu wanu ndi kuonetsetsa kuti mukutsatira malamulo ake onse ndi mfundo zake zimene ndikukupatsani lero, matemberero otsatirawa adzakugwerani ndi kukupezani:+
27 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira dziko limeneli mwa kulibweretsera matemberero onse olembedwa m’buku ili.+
15 Mawu onse abwino amene Yehova Mulungu wanu analankhula akwaniritsidwa pa inu,+ momwemonso Yehova adzakwaniritsa pa inu mawu onse oipa, kufikira atakufafanizani kukuchotsani padziko labwinoli, limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.+
27 Koma Yehova anati: “Yuda+ nayenso ndim’chotsa pamaso panga+ monga mmene ndinachotsera Isiraeli,+ ndipo ndithu ndidzakana ngakhale mzinda wa Yerusalemu umene ndinausankha, ndi nyumba imene ndinanena kuti, ‘Dzina langa lizikhala pamenepo.’”+
3 “‘Ndidzawagwetsera masoka a mitundu inayi,’+ watero Yehova. ‘Ndidzawatumizira lupanga kuti liwaphe, agalu kuti akoke mitembo yawo, zolengedwa zouluka zam’mlengalenga+ ndi zilombo zakutchire kuti ziwadye ndi kuwawononga.
12 Chotero Ziyoni adzagawulidwa ngati munda chifukwa cha anthu inu ndipo Yerusalemu adzangokhala milu ya mabwinja.+ Phiri la nyumba ya Mulungu lidzakhala ngati zitunda za m’nkhalango.