-
2 Mbiri 36:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 Kumayambiriro+ kwa chaka, Mfumu Nebukadinezara inatuma+ asilikali ake omwe anakamutenga n’kubwera naye ku Babulo+ limodzi ndi zinthu zabwinozabwino za m’nyumba ya Yehova.+ Kuwonjezera apo, Nebukadinezara analonga ufumu Zedekiya+ yemwe anali m’bale wa bambo ake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.+
-
-
Yeremiya 22:30Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
30 Yehova wanena kuti, ‘Lembani kuti munthu uyu alibe ana,+ munthu wamphamvu amene zinthu sizidzamuyendera bwino m’masiku a moyo wake. Pakuti mwa ana ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe amene zinthu zidzamuyendera bwino.+ Palibe ngakhale mmodzi amene adzakhala pampando wachifumu wa Davide+ ndi kulamulira mu Yuda.’”
-