10 “Bwerani mudzaukire mizere yake ya mitengo ya mpesa ndi kuiwononga,+ koma anthu inu musaifafaniziretu.+ M’chotsereni mphukira zake zamasamba ambiri chifukwa si za Yehova.+
11 “Pakuti ine ndili ndi iwe kuti ndikupulumutse,”+ watero Yehova. “Ndidzawononga anthu a mitundu yonse ya kumene ndinakubalalitsirani,+ koma iwe sindidzakuwononga.+ Ndidzakuwongolera pa mlingo woyenera chifukwa sindidzakusiya osakulanga.”+