Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ezekieli 6:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Opulumuka anu akadzagwidwa n’kutengedwa kukakhala pakati pa mitundu ina ya anthu, ndithu adzandikumbukira.+ Adzakumbukira mmene ndinamvera kupweteka chifukwa cha mtima wawo wadama umene unawachititsa kundipandukira.+ Adzakumbukiranso mmene ndinamvera kupweteka chifukwa cha maso awo othamangira mafano awo onyansa pofuna kuchita nawo zadama.+ Iwo adzachita manyazi ochita kuonekera pankhope zawo, chifukwa cha zinthu zonse zoipa ndi zonyansa zimene anachita.+

  • Ezekieli 20:43
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 43 Ndithu kumeneko mudzakumbukira njira zanu+ ndi zochita zanu zonse zimene munali kudziipitsa nazo.+ Mukadzakumbukira zimenezi, mudzachita manyazi ochita kuonekera pankhope zanu chifukwa cha zoipa zonse zimene munachita.+

  • Zekariya 12:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 “Posonyeza kuti ndakomera mtima nyumba ya Davide ndi anthu okhala mu Yerusalemu, ndidzawapatsa mzimu wanga+ umene udzawalimbikitse kundipempha mochonderera.+ Ndithu iwo adzayang’ana kwa munthu amene anamulasa,+ ndipo adzamulirira ngati mmene amachitira polirira mwana yekhayo wamwamuna. Adzamulira mowawidwa mtima ngati mmene amachitira polira maliro a mwana wamwamuna woyamba kubadwa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena