Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nehemiya 9:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Choncho iwo anakana kumvera+ ndipo sanakumbukire+ zochita zanu zodabwitsa zimene munawachitira, m’malomwake anaumitsa khosi lawo+ ndipo anasankha mtsogoleri+ kuti awatsogolere pobwerera ku ukapolo wawo ku Iguputo. Koma inu ndinu Mulungu wokhululuka,+ wachisomo+ ndi wachifundo,+ wosakwiya msanga+ ndiponso wosonyeza kukoma mtima kosatha,+ chotero simunawasiye.+

  • Salimo 86:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Koma inu Yehova, ndinu Mulungu wachifundo ndi wachisomo,+

      Wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha ndi choonadi.+

  • Salimo 103:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  8 Yehova ndi wachifundo ndi wachisomo,+

      Wosakwiya msanga ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha.+

  • Yona 4:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Choncho iye anapemphera kwa Yehova kuti: “Inu Yehova, kodi zimene ndimaopa ndili kwathu zija si zimenezi? N’chifukwa chaketu ine ndinathawa kupita ku Tarisi.+ Ndinadziwa kuti inu ndinu Mulungu wachisomo ndi wachifundo,+ wosakwiya msanga, wodzaza ndi kukoma mtima kosatha+ komanso mumatha kusintha maganizo pa tsoka limene mumafuna kubweretsa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena