11 “Solomo anali ndi munda wa mpesa+ ku Baala-hamoni. Munda wa mpesawo anaupereka kwa anthu oti aziusamalira.+ Munthu aliyense anali kubweretsa ndalama zasiliva zokwana 1,000 zolipirira zipatso za mundawo.
5Ndikufuna ndimuimbire nyimbo munthu amene ndimamukonda. Imeneyi ndi nyimbo yonena za munthu amene ndimamukonda, ndiponso munda wake wa mpesa.+ Wokondedwa wanga anali ndi munda wa mpesa pamalo achonde m’mbali mwa phiri.