18 Koma Paulo atakhala kumeneko masiku ndithu, anatsanzikana ndi abalewo ndipo anapitiriza ulendo wake wa pamadzi kulowera ku Siriya. Pa ulendowu anatsagana ndi Purisikila ndi Akula. Paulo anameta tsitsi lake+ ku Kenkereya+ chifukwa cha lonjezo limene anachita.