Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 9:15, 16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Pofika pano ndikanakhala nditatambasula kale dzanja langa nʼkupha iweyo komanso anthu ako ndi mliri woopsa, ndipo ndikanakufafanizani padziko lapansi. 16 Koma ndakusiya ndi moyo kuti ndikusonyeze mphamvu zanga komanso kuti dzina langa lilengezedwe padziko lonse lapansi.+

  • Ekisodo 15:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ndi mulungu uti amene angafanane nanu, inu Yehova?+

      Mumasonyeza kuti ndinu woyera koposa,+ ndani angafanane ndi inu?

      Ndinu woyenera kuopedwa ndi kukuimbirani nyimbo zotamanda. Inu mumachita zodabwitsa.+

  • Ekisodo 18:10, 11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndiyeno Yetero anati: “Yehova atamandike, amene anakupulumutsani ku Iguputo ndiponso kwa Farao, amenenso analanditsa anthuwa kwa Aiguputo omwe ankawazunza. 11 Tsopano ndadziwa kuti Yehova ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse,+ chifukwa cha zimene anachitira anthu amene ankachita zinthu modzikuza pamaso pa anthu ake.”

  • Yoswa 2:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Ndipo anawauza kuti: “Ndikudziwa kuti Yehova akupatsani dzikoli+ ndipo tonse tikuchita nanu mantha.+ Aliyense mʼdzikoli mtima wake suli mʼmalo chifukwa cha inu.+ 10 Tinamva mmene Yehova anaphwetsera madzi a Nyanja Yofiira pamene munkachoka ku Iguputo.+ Komanso mmene munaphera mafumu awiri a Aamori, Sihoni+ ndi Ogi,+ kutsidya* kwa mtsinje wa Yorodano.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena