Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 20:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Munthu amene wachita zosakhulupirika* podalira anthu olankhulana ndi mizimu+ komanso olosera zamʼtsogolo,+ ndidzadana naye ndithu ndipo ndidzamupha kuti asakhalenso pakati pa anthu a mtundu wake.+

  • Deuteronomo 18:10-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Pakati panu pasapezeke munthu wowotcha mwana wake pamoto,*+ wolosera,+ aliyense wochita zamatsenga,+ aliyense woombeza,+ wanyanga,+ 11 aliyense wochesula* ena, aliyense wofunsira kwa wolankhula ndi mizimu+ kapena wolosera zamʼtsogolo,+ kapena aliyense wofunsira kwa akufa.+ 12 Chifukwa aliyense wochita zimenezi ndi wonyansa kwa Yehova. Ndipo chifukwa chakuti anthu a mitundu ina akuchita zimenezi, Yehova Mulungu wanu akuwathamangitsa pamaso panu.

  • 1 Mbiri 10:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Choncho Sauli anafa chifukwa chakuti anasonyeza kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanamvere mawu a Yehova+ komanso anapita kukafunsa kwa wolankhula ndi mizimu+

  • Yesaya 8:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Ndipo atakuuzani kuti: “Funsirani kwa anthu olankhula ndi mizimu kapena anthu olosera zamʼtsogolo, omwe amalira ngati mbalame ndiponso kulankhula motsitsa mawu,” kodi mungavomere? Kodi mtundu uliwonse wa anthu suyenera kufunsira kwa Mulungu wake? Kodi akuyenera kufunsira kwa anthu akufa pofuna kuthandiza anthu amoyo?+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena