Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 61:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 61 Mzimu wa Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, uli pa ine,+

      Chifukwa Yehova anandidzoza kuti ndilengeze uthenga wabwino kwa anthu ofatsa.+

      Anandituma kuti ndikamange mabala a anthu osweka mtima,

      Kuti ndilengeze za ufulu kwa anthu amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,

      Komanso kuti maso a akaidi adzatsegulidwa.+

       2 Wandituma kuti ndilengeze za chaka cha Yehova chokomera anthu mtima,*

      Ndi za tsiku lobwezera la Mulungu wathu,+

      Komanso kuti nditonthoze anthu onse amene akulira,+

  • Luka 4:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 “Mzimu wa Yehova* uli pa ine, chifukwa iye anandidzoza kuti ndilengeze uthenga wabwino kwa anthu osauka. Anandituma kudzalengeza za ufulu kwa anthu amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina komanso zoti akhungu ayambe kuona. Anandituma kudzamasula oponderezedwa kuti akhale pa ufulu,+ 19 ndi kudzalalikira za chaka chovomerezeka kwa Yehova.”*+

  • Aroma 8:20, 21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Popeza chilengedwe chinaweruzidwa kuti chikhale chopanda pake,+ osati mwa kufuna kwake koma kudzera mwa amene anachiweruza. Ndipo anaperekanso chiyembekezo 21 chakuti chilengedwecho chidzamasulidwa+ ku ukapolo wa thupi limene limawonongeka nʼkukhala ndi ufulu waulemerero wa ana a Mulungu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena