Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 7:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 “‘Lamulo la nsembe yakupalamula+ ndi ili: Nsembeyi ndi yopatulika koposa.

  • Levitiko 14:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Ili likhale lamulo lokhudza wakhate pa tsiku limene adzamubweretse kwa wansembe+ pa nthawi yoti ayeretsedwe.

  • Levitiko 14:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Wansembeyo azidzatenga nkhosa yaingʼono yamphongo imodzi nʼkuipereka monga nsembe yakupalamula+ pamodzi ndi muyezo umodzi wa mafuta uja. Zimenezi aziziyendetsa uku ndi uku monga nsembe yoperekedwa kwa Yehova.+

  • Levitiko 19:20, 21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Mwamuna akagona ndi kapolo wamkazi amene mbuye wake anamulonjeza kuti adzamupereka kwa mwamuna wina, koma mkaziyo sanawomboledwe kapena kupatsidwa ufulu, pazikhala chilango. Koma iwo asaphedwe chifukwa mkaziyo anali asanakhale mfulu. 21 Mwamunayo azibweretsa kwa Yehova nkhosa yamphongo ya nsembe yakupalamula pakhomo la chihema chokumanako.+

  • Numeri 6:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Munthuyo aziyambiranso masiku ake odzipereka kwa Yehova ngati Mnaziri, ndipo azibweretsa nkhosa yaingʼono yamphongo yosapitirira chaka chimodzi monga nsembe yakupalamula. Koma masiku oyamba aja sadzawerengedwa chifukwa anadetsa unaziri wake.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena