Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 29:27, 28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Pankhosa yoikira Aroni ndi ana ake kuti akhale ansembe, upatule chidale cha nsembe yoyendetsa uku ndi uku, ndi mwendo wa gawo lopatulika umene anapereka.+ 28 Zimenezi zikhale za Aroni ndi ana ake mwa lamulo mpaka kalekale. Aisiraeli ayenera kutsatira lamulo limeneli chifukwa ndi gawo lopatulika. Lidzakhala gawo lopatulika loyenera kuperekedwa ndi Aisiraeli.+ Limeneli ndi gawo lawo lopatulika loperekedwa kwa Yehova kuchokera pansembe zawo zamgwirizano.+

  • Numeri 18:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Yehova anapitiriza kulankhula ndi Aroni kuti: “Ine ndakupatsa udindo woyangʼanira zinthu zonse zimene anthu azipereka kwa ine.+ Pa zinthu zonse zopatulika zimene Aisiraeli azipereka, ndakupatsa gawo iweyo ndi ana ako, kuti likhale lanu mpaka kalekale.+

  • Deuteronomo 18:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Tsopano zinthu zimene ansembe azidzalandira kuchokera kwa anthu ndi izi: Amene akupereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe mwendo wakutsogolo, nsagwada ndi chifu.

  • Ezekieli 44:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Iwowa ndi amene azidzadya nsembe yambewu,+ nsembe yamachimo ndi nsembe yakupalamula+ ndipo chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mu Isiraeli chidzakhala chawo.+

  • 1 Akorinto 9:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Kodi simukudziwa kuti anthu amene amagwira ntchito zopatulika amadya zamʼkachisi, ndipo amene amatumikira kuguwa lansembe nthawi zonse amalandira zina mwa zinthu zoperekedwa paguwa lansembelo?+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena