-
Oweruza 14:5, 6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
5 Choncho Samisoni anapita ku Timuna pamodzi ndi bambo ndi mayi ake. Atafika mʼminda ya mpesa ya ku Timuna, anakumana ndi mkango ndipo unayamba kubangula. 6 Ndiyeno mzimu wa Yehova unamupatsa mphamvu,+ moti anakhadzula mkangowo pakati ngati mmene munthu angakhadzulire kamwana ka mbuzi ndi manja. Koma sanauze bambo kapena mayi ake zimene anachitazi.
-