Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 24:7-9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Pagulu lililonse la mikateyo uike lubani weniweni. Lubaniyo aziperekedwa nsembe yowotcha pamoto+ kwa Yehova kuimira nsembe yonseyo. 8 Pa tsiku lililonse la Sabata azikhazika mkatewo pamaso pa Yehova nthawi zonse.+ Limeneli ndi pangano pakati pa ine ndi Aisiraeli mpaka kalekale. 9 Mkatewo uzikhala wa Aroni ndi ana ake,+ ndipo aziudyera mʼmalo oyera,+ chifukwa waperekedwa kwa iye monga chinthu choyera koposa kuchokera pa nsembe zowotcha pamoto zoperekedwa kwa Yehova. Limeneli likhale lamulo mpaka kalekale.”

  • Maliko 2:25, 26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Koma iye anawayankha kuti: “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita, iyeyo ndi amuna omwe anali naye atamva njala ndipo analibiretu chilichonse?+ 26 Nkhani yonena za Abiyatara+ wansembe wamkulu imanena kuti, Davide analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo anadya mitanda ya mkate woonetsa kwa Mulungu,* umene aliyense sankayenera kudya malinga ndi malamulo koma ansembe okha.+ Iye anatenga mitanda ina ya mkatewo nʼkupatsa amuna amene anali naye limodzi. Kodi inu simunawerenge nkhani imeneyi?”

  • Luka 6:3, 4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Koma Yesu anawayankha kuti: “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita, iyeyo ndi amuna omwe anali naye atamva njala?+ 4 Kodi simunawerenge kuti analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo anadya mitanda ya mkate woonetsa kwa Mulungu,* imene iye ndi anthu omwe anali nawo aja sankayenera kudya malinga ndi malamulo, koma ansembe okha?”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena