Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 14:1-7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Munthu wopusa* amanena mumtima mwake kuti:

      “Kulibe Yehova.”+

      Zochita za anthu amenewa ndi zoipa komanso zonyansa,

      Ndipo palibe amene akuchita zabwino.+

       2 Koma kuchokera kumwamba, Yehova amayangʼana ana a anthu,

      Kuti aone ngati pali aliyense wozindikira, ngati pali aliyense amene akufunafuna Yehova.+

       3 Onse apatuka,+

      Ndipo onsewo ndi achinyengo.

      Palibe aliyense amene akuchita zabwino,

      Palibiretu ndi mmodzi yemwe.

       4 Kodi palibe aliyense womvetsa zinthu pakati pa anthu ochita zoipawa?

      Iwo amadya anthu anga ngati kuti akudya chakudya.

      Ndipo sapemphera kwa Yehova.

       5 Koma adzagwidwa ndi mantha aakulu,+

      Chifukwa Yehova ali pakati pa mʼbadwo wa anthu olungama.

       6 Inu anthu ochita zoipa mumayesetsa kusokoneza mapulani a munthu wonyozeka,

      Koma Yehova ndi malo ake othawirako.+

       7 Zikanakhala bwino chipulumutso cha Isiraeli chikanachokera ku Ziyoni.+

      Yehova akadzabwezeretsa anthu ake amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,

      Yakobo adzasangalale, Isiraeli adzakondwere.

  • Aroma 3:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 mogwirizana ndi zimene Malemba amanena kuti: “Palibe munthu wolungama ndi mmodzi yemwe.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena